< Zekariya 12 >

1 Uthenga wa Yehova kwa Israeli. Yehova, amene amayala mlengalenga, amene amayika maziko a dziko lapansi, ndiponso amene amalenga mzimu wokhala mwa munthu, akunena kuti,
Břímě slova Hospodinova příčinou Izraele. Praví Hospodin, kterýž roztáhl nebesa, a založil zemi, a sformoval ducha člověka, kterýž jest v něm:
2 “Taonani, ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala chakumwa choledzeretsa chimene chidzasokoneza mitundu yonse ya anthu yomuzungulira. Yuda adzazingidwa pamodzinso ndi Yerusalemu.
Aj, já postavím Jeruzalém jako číši, kteráž ku potácení přivede všecky národy vůkol, kteříž budou proti Judovi v obležení, i proti Jeruzalému.
3 Pa tsiku limenelo, pamene mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi idzasonkhana kulimbana naye, ndidzasandutsa Yerusalemu thanthwe losatheka kusunthidwa ndi mitundu yonse ya anthu. Onse oyesa kumusuntha adzadzipweteka.
Nýbrž stane se v ten den, že položím Jeruzalém jako kámen přetěžký všechněm národům, jejž kdožkoli zdvihati budou, velmi se urazí, byť se pak shromáždili proti němu všickni národové země.
4 Pa tsiku limenelo kavalo aliyense ndidzamuchititsa mantha kuti asokonezeke, ndipo wokwerapo wake ndidzamuchititsa misala,” akutero Yehova. “Ndidzayangʼanira nyumba ya Yuda koma ndidzachititsa khungu akavalo onse a anthu a mitundu ina.
V ten den, praví Hospodin, raním všelikého koně strnutím, a jezdce jeho zblázněním, ale na dům Judský otevru oči své, a všecky koně národů raním slepotou.
5 Pamenepo atsogoleri a Yuda adzayankhula mʼmitima mwawo kuti, ‘Anthu a ku Yerusalemu ndi amphamvu, chifukwa Yehova Wamphamvuzonse ndiye Mulungu wawo.’
I dějí vůdcové Judští v srdci svém: Mámeť sílu, i obyvatelé Jeruzalémští, v Hospodinu zástupů, Bohu svém.
6 “Pa tsiku limenelo ndidzasandutsa atsogoleri a Yuda kukhala ngati mbawula yotentha pakati pa nkhuni, ngati sakali yoyaka pa mitolo ya tirigu. Adzatentha mitundu yonse ya anthu yowazungulira, kumanja ndi kumanzere, koma Yerusalemu sadzasuntha pa malo ake.
V ten den učiním vůdce Judské podobné ohni zanícenému mezi dřívím, a pochodni hořící mezi snopy, i zžíře na pravo i na levo všecky národy vůkol, a ostojí Jeruzalém ještě na místě svém v Jeruzalémě.
7 “Yehova adzapulumutsa malo okhala Yuda poyamba, kuti ulemu wa nyumba ya Davide ndi wa anthu okhala mu Yerusalemu usapambane ulemu wa Yuda.
Zachová Hospodin i stánky Judské prvé, aby se nevelebila ozdoba domu Davidova a ozdoba, přebývajících v Jeruzalémě nad Judu.
8 Pa tsiku limenelo Yehova adzatchinjiriza onse okhala mu Yerusalemu, kotero kuti anthu ofowoka kwambiri pakati pawo adzakhala ngati Davide, ndipo nyumba ya Davide idzakhala ngati Mulungu, ngati mngelo wa Yehova wowatsogolera.
V ten den chrániti bude Hospodin obyvatelů Jeruzalémských, a bude nejnestatečnější z nich v ten den podobný Davidovi, a dům Davidův podobný bohům, podobný andělu Hospodinovu před nimi.
9 Pa tsiku limenelo ndidzawononga mitundu yonse yofuna kuthira nkhondo Yerusalemu.
Nebo stane se v ten den, že shledám všecky národy, kteříž přitáhnou proti Jeruzalému, abych je zahladil.
10 “Ndipo pa nyumba ya Davide ndi pa anthu okhala mu Yerusalemu ndidzakhuthulirapo mzimu wachisomo ndi wopemphera. Iwo adzandiyangʼana Ine, amene anamubaya, ndipo adzamulirira kwambiri monga momwe munthu amalirira mwana wake mmodzi yekhayo, ndiponso adzamva chisoni kwambiri monga momwe amachitira ndi mwana woyamba kubadwa.
A vyleji na dům Davidův a na obyvatele Jeruzalémské Ducha milosti a pokorných proseb. I obrátí zřetel ke mně, kteréhož jsou bodli, a kvíliti budou nad ním jako kvílením nad jednorozeným; hořce, pravím, plakati budou nad ním, jako hořce plačí nad prvorozeným.
11 Pa tsiku limenelo mudzakhala kulira kwakukulu mu Yerusalemu, monga kulira kwa ku Hadadi-Rimoni ku chigwa cha Megido.
V ten den bude veliké kvílení v Jeruzalémě, jako kvílení v Adadremmon na poli Mageddo.
12 Dziko lidzalira kwambiri, fuko lililonse pa lokha, akazi awo pa okhanso: fuko la Davide pamodzi ndi akazi awo, fuko la Natani pamodzi ndi akazi awo,
Nebo kvíliti bude země, každá čeled obzvláštně, čeled domu Davidova obzvláštně, a ženy jejich obzvláštně, čeled domu Nátanova obzvláštně, a ženy jejich obzvláštně,
13 nyumba ya Levi pamodzi ndi akazi awo, fuko la Simei pamodzi ndi akazi awo,
Èeled domu Léví obzvláštně, a ženy jejich obzvláštně, čeled Semei obzvláštně, a ženy jejich obzvláštně,
14 ndiponso mafuko onse pamodzi ndi akazi awo.
I všecky čeledi jiné, každá čeled obzvláštně, a ženy jejich obzvláštně.

< Zekariya 12 >