< Zekariya 11 >

1 Tsekula zitseko zako, iwe Lebanoni, kuti moto unyeketse mikungudza yako!
Отвори, Ливане, врата своја, и огањ нека прождре кедре твоје.
2 Lira mwachisoni, iwe mtengo wa payini, pakuti mkungudza wagwa; mtengo wamphamvu wawonongeka! Lirani mwachisoni, inu mitengo ya thundu ya Basani; nkhalango yowirira yadulidwa!
Ридај, јело, јер паде кедар, јер красници пропадоше; ридајте, храстови васански, јер се посече шума ограђена.
3 Imvani kulira mwachisoni kwa abusa; msipu wawo wobiriwira wawonongeka! Imvani kubangula kwa mikango; nkhalango yowirira ya ku Yorodani yawonongeka!
Стоји јаук пастира, јер се затре слава њихова; стоји рика лавова, јер се опустоши понос јордански.
4 Yehova Mulungu wanga akuti, “Dyetsa nkhosa zimene zikukaphedwa.
Овако вели Господ Бог мој: Паси овце кланице,
5 Amene amagula nkhosazo amazipha ndipo salangidwa. Amene amazigulitsa amanena kuti, ‘Alemekezeke Yehova, ine ndalemera!’ Abusa ake omwe sazimvera chisoni nkhosazo.
Које убијају они који их држе, нити их ко криви, и који их продају говоре: Благословен да је Господ, обогатих се; и који их пасу, ниједан их не жали.
6 Pakuti Ine sindidzamveranso chisoni anthu okhala mʼdziko,” akutero Yehova. “Ndidzapereka munthu aliyense mʼmanja mwa mnansi wake ndi mwa mfumu yake. Iwo adzazunza dziko, ndipo Ine sindidzawapulumutsa mʼmanja mwawo.”
Зато нећу више жалити становника земаљских, говори Господ, него ћу, ево предати једног другом у руке и у руке цару њиховом, и они ће потрти земљу, а ја је нећу избавити из руку њихових.
7 Choncho ine ndinadyetsa nkhosa zokaphedwa, makamaka nkhosa zoponderezedwa. Pamenepo ndinatenga ndodo ziwiri ndipo yoyamba ndinayitcha Kukoma mtima ndipo yachiwiri ndinayitcha Umodzi ndipo ndinadyetsa nkhosazo.
И пасох овце кланице, невољне од стада, и узевши два штапа назвах један благост, а други назвах свеза, и пасох стадо.
8 Pa mwezi umodzi ndinachotsa abusa atatu. Abusawo anadana nane, ndipo ndinatopa nawo.
И погубих три пастира за месец дана, јер се душа моја љућаше на њих, и душа њихова мржаше на ме.
9 Ndinawuza gulu la nkhosalo kuti, “Sindidzakhalanso mʼbusa wanu. Imene ikufa, ife, ndipo imene ikuwonongeka, iwonongeke, zimene zatsala zizidyana.”
И рекох: Нећу вас више пасти; која погине нека погине, и која пропадне нека пропадне, и које остану нека једу месо једна другој.
10 Kenaka ndinatenga ndodo yanga yotchedwa Kukoma mtima ndi kuyithyola, kuphwanya pangano limene ndinachita ndi mitundu yonse ya anthu.
И узех свој штап, благост, и сломих га да укинем завет свој који учиних са свим народима.
11 Linaphwanyidwa tsiku limenelo ndipo nkhosa zosautsidwa zimene zimandiyangʼanitsitsa zinadziwa kuti anali mawu a Yehova.
И укиде се оног дана, и невољни од стада, који гледаху на ме, познаше доиста да беше реч Господња.
12 Ndinawawuza kuti, “Ngati mukuganiza kuti zili bwino, patseni malipiro anga; koma ngati si choncho, sungani malipirowo.” Kotero anandipatsa ndalama zasiliva makumi atatu.
И рекох им: Ако вам је драго, дајте ми моју плату; ако ли није немојте; и измерише ми плату, тридесет сребрника.
13 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ziponye kwa wowumba mbiya,” mtengo woyenera umene anapereka pondigula Ine! Choncho ndinatenga ndalama zasiliva makumi atatu ndi kuziponya mʼnyumba ya Yehova kwa wowumba mbiya.
И рече ми Господ: Баци лончару ту часну цену којом ме проценише. И узевши тридесет сребрника бацих их у дом Господњи лончару.
14 Kenaka ndinathyola ndodo yanga yachiwiri yotchedwa Umodzi, kuthetsa ubale pakati pa Yuda ndi Israeli.
Потом сломих други штап свој, свезу, да укинем братство између Јуде и Израиља.
15 Pamenepo Yehova anayankhula nane kuti, “Tenganso zida za mʼbusa wopusa.
И Господ ми рече: Узми јоште оправу безумног пастира.
16 Pakuti ndidzawutsa mʼbusa mʼdzikomo amene sadzasamalira zotayika, kapena kufunafuna zazingʼono, kapena zovulala, kapena kudyetsa nkhosa zabwino, koma iye adzadya nyama ya nkhosa zonenepa, nʼkumakukuta ndi ziboda zomwe.
Јер ево ја ћу подигнути пастира у земљи, који неће обилазити оне који гину, неће тражити нејаке, нити ће лечити рањене, нити ће носити сустале, него ће јести месо од претилих, и папке ће им кидати.
17 “Tsoka kwa mʼbusa wopandapake, amene amasiya nkhosa! Lupanga limukanthe pa mkono wake ndi pa diso lake lakumanja! Mkono wake ufote kotheratu, diso lake lamanja lisaonenso.”
Тешко пастиру никаквом, који оставља стадо! Мач му је над мишицом и над десним оком; мишица ће му усахнути и десно ће му око потамнети.

< Zekariya 11 >