< Zekariya 11 >

1 Tsekula zitseko zako, iwe Lebanoni, kuti moto unyeketse mikungudza yako!
Vula iminyango yakho, wena Lebhanoni, ukuze umlilo udle imisedari yakho.
2 Lira mwachisoni, iwe mtengo wa payini, pakuti mkungudza wagwa; mtengo wamphamvu wawonongeka! Lirani mwachisoni, inu mitengo ya thundu ya Basani; nkhalango yowirira yadulidwa!
Qhinqa isililo, wena sihlahla sefiri; ngoba umsedari usuwile, ngoba izihlahla zobukhosi ziyachithwa. Qhinqani isililo lina ma-okhi eBashani, ngoba igusu elingangenekiyo seliwile.
3 Imvani kulira mwachisoni kwa abusa; msipu wawo wobiriwira wawonongeka! Imvani kubangula kwa mikango; nkhalango yowirira ya ku Yorodani yawonongeka!
Kulelizwi lokuqhinqa isililo kwabelusi, ngoba udumo lwabo luyachithwa; ilizwi lokubhonga kwamabhongo ezilwane, ngoba ukuziqhenya kweJordani kuyachithwa.
4 Yehova Mulungu wanga akuti, “Dyetsa nkhosa zimene zikukaphedwa.
Itsho njalo iNkosi uNkulunkulu wami: Yelusa izimvu zokuhlatshwa;
5 Amene amagula nkhosazo amazipha ndipo salangidwa. Amene amazigulitsa amanena kuti, ‘Alemekezeke Yehova, ine ndalemera!’ Abusa ake omwe sazimvera chisoni nkhosazo.
abathengi bazo bayazibulala, bathi kabalacala; labazithengisayo bathi: Kayibusiswe iNkosi; ngoba nginothile; labelusi bazo kabalasihawu ngazo.
6 Pakuti Ine sindidzamveranso chisoni anthu okhala mʼdziko,” akutero Yehova. “Ndidzapereka munthu aliyense mʼmanja mwa mnansi wake ndi mwa mfumu yake. Iwo adzazunza dziko, ndipo Ine sindidzawapulumutsa mʼmanja mwawo.”
Ngoba kangisayikuyekela abahlali belizwe, itsho iNkosi; kodwa khangela, ngizanikela abantu, ngulowo lalowo esandleni sikamakhelwane wakhe, lesandleni senkosi yakhe; njalo bazaliphahlaza ilizwe, njalo kangiyikubophula esandleni sabo.
7 Choncho ine ndinadyetsa nkhosa zokaphedwa, makamaka nkhosa zoponderezedwa. Pamenepo ndinatenga ndodo ziwiri ndipo yoyamba ndinayitcha Kukoma mtima ndipo yachiwiri ndinayitcha Umodzi ndipo ndinadyetsa nkhosazo.
Njalo ngizakwelusa izimvu zokuhlatshwa, isibili, eziyangekileyo zezimvu. Njalo ngazithathela intonga ezimbili; enye ngayibiza ngokuthi nguBuhle, lenye ngayibiza ngokuthi nguZibopho; ngazelusa izimvu.
8 Pa mwezi umodzi ndinachotsa abusa atatu. Abusawo anadana nane, ndipo ndinatopa nawo.
Ngasengiquma abelusi abathathu ngenyanga eyodwa; lomphefumulo wami wadabuka ngabo, lomphefumulo wabo lawo wangenyanya.
9 Ndinawuza gulu la nkhosalo kuti, “Sindidzakhalanso mʼbusa wanu. Imene ikufa, ife, ndipo imene ikuwonongeka, iwonongeke, zimene zatsala zizidyana.”
Ngasengisithi: Kangisayikulelusa; ofayo kafe, loqunywayo kaqunywe; kakuthi-ke abaseleyo badle, ngulowo lalowo inyama yomunye.
10 Kenaka ndinatenga ndodo yanga yotchedwa Kukoma mtima ndi kuyithyola, kuphwanya pangano limene ndinachita ndi mitundu yonse ya anthu.
Ngasengithatha intonga yami, uBuhle, ngayiqamula, ukuze ngephule isivumelwano sami engangisenze labantu bonke.
11 Linaphwanyidwa tsiku limenelo ndipo nkhosa zosautsidwa zimene zimandiyangʼanitsitsa zinadziwa kuti anali mawu a Yehova.
Sephulwa-ke ngalolosuku; ngakho-ke eziyangekileyo zezimvu ezazilindele kimi zakwazi ukuthi yilizwi leNkosi.
12 Ndinawawuza kuti, “Ngati mukuganiza kuti zili bwino, patseni malipiro anga; koma ngati si choncho, sungani malipirowo.” Kotero anandipatsa ndalama zasiliva makumi atatu.
Ngasengisithi kizo: Uba kulungile emehlweni enu, nikani inkokhelo yami; kodwa uba kungenjalo, yekelani. Basebelinganisela inkokhelo yami, inhlamvu ezingamatshumi amathathu zesiliva.
13 Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ziponye kwa wowumba mbiya,” mtengo woyenera umene anapereka pondigula Ine! Choncho ndinatenga ndalama zasiliva makumi atatu ndi kuziponya mʼnyumba ya Yehova kwa wowumba mbiya.
INkosi yasisithi kimi: Ziphosele kumbumbi; intengo enkulu ebengiyilinganiselwe yibo! Ngasengithatha inhlamvu ezingamatshumi amathathu zesiliva, ngaziphosela kumbumbi endlini yeNkosi.
14 Kenaka ndinathyola ndodo yanga yachiwiri yotchedwa Umodzi, kuthetsa ubale pakati pa Yuda ndi Israeli.
Ngasengiqamula intonga yami yesibili, uZibopho, ukuze ngephule ubuzalwane phakathi kukaJuda loIsrayeli.
15 Pamenepo Yehova anayankhula nane kuti, “Tenganso zida za mʼbusa wopusa.
INkosi yasisithi kimi: Zithathele futhi izikhali zomelusi oyisithutha.
16 Pakuti ndidzawutsa mʼbusa mʼdzikomo amene sadzasamalira zotayika, kapena kufunafuna zazingʼono, kapena zovulala, kapena kudyetsa nkhosa zabwino, koma iye adzadya nyama ya nkhosa zonenepa, nʼkumakukuta ndi ziboda zomwe.
Ngoba khangela, ngizavusa umelusi elizweni; ongayikuhambela eziqunyiweyo, ongayikudinga ezintsha, ongayikwelapha ezephukileyo, ongayikusekela ezizimeleyo; kodwa adle inyama yezinonileyo, adabule iziqa amasondo azo.
17 “Tsoka kwa mʼbusa wopandapake, amene amasiya nkhosa! Lupanga limukanthe pa mkono wake ndi pa diso lake lakumanja! Mkono wake ufote kotheratu, diso lake lamanja lisaonenso.”
Maye kumelusi ongasizi lutho otshiya izimvu! Inkemba izakuba phezu kwengalo yakhe, laphezu kwelihlo lakhe lokunene. Ingalo yakhe izatshwabhana isibili, lelihlo lakhe lokunene lifiphale ngokupheleleyo.

< Zekariya 11 >