< Zekariya 10 >

1 Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira; ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula. Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu, ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
Proście PANA o deszcz w późnej porze [deszczowej], a PAN stworzy chmury burzowe i da wam obfity deszcz i każdemu trawę na polu.
2 Mafano amayankhula zachinyengo, owombeza mawula amaona masomphenya abodza; amafotokoza maloto onama, amapereka chitonthozo chopandapake. Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika chifukwa chosowa mʼbusa.
Bożki wypowiadają bowiem [słowa] próżności, a wróżbici prorokują kłamstwo i opowiadają zmyślone sny, daremnie pocieszają. Dlatego błąkali się jak trzoda, byli utrapieni, bo nie było pasterza.
3 “Ine ndawakwiyira kwambiri abusa, ndipo ndidzalanga atsogoleri; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira nkhosa zake, nyumba ya Yuda, ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
Mój gniew zapłonął przeciwko tym pasterzom i ukarałem te kozły, ale PAN zastępów nawiedzi swoją trzodę, dom Judy, i uczyni z niej wspaniałego konia do boju.
4 Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya, mudzachokera chikhomo cha tenti, mudzachokera uta wankhondo, mudzachokera mtsogoleri aliyense.
Od niego wywodzi się kamień węgielny, od niego gwóźdź, od niego łuk wojenny, od niego także wszelki poborca.
5 Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo. Chifukwa Yehova adzakhala nawo, adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.
I będą jak mocarze, którzy wdeptują wroga w błoto uliczne podczas bitwy. I będą walczyć, bo PAN [jest] z nimi; a zawstydzą jeźdźców konnych.
6 “Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe. Ndidzawabwezeretsa chifukwa ndawamvera chisoni. Adzakhala ngati kuti sindinawakane, chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.
Umocnię dom Judy, wybawię dom Józefa i sprowadzę ich z powrotem w pokoju, bo zlituję się nad nimi. I będą [takimi], jak gdybym ich nie odrzucił. Ja bowiem jestem PAN, ich Bóg, i wysłucham ich.
7 Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo. Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala; mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
Efraimici będą jak mocarz, ich serce rozweseli się jak od wina. Ich synowie to zobaczą i będą się cieszyć, a ich serce rozraduje się w PANU.
8 Ndidzaliza mluzu ndi kuwasonkhanitsa pamodzi. Ndithu ndawawombola; adzachulukana ngati poyamba paja.
Zaświstam na nich i zgromadzę ich, bo ich odkupiłem; i będą tak liczni, jak byli [dawniej].
9 Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu, koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira. Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka, ndipo adzabwerera.
I rozsieję ich wśród narodów, aby w dalekich krajach przypomnieli sobie o mnie, a żyjąc tam ze swoimi dziećmi, nawrócą się.
10 Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya. Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni, mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
Wyprowadzę ich znowu z ziemi Egiptu i zgromadzę ich z Asyrii, zaprowadzę do ziemi Gilead i do Libanu, ale nie starczy dla nich [miejsca].
11 Adzawoloka nyanja ya masautso; nyanja yokokoma idzagonja ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa. Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
Przejdzie przez morze ucisku, rozbije fale na morzu i wyschną wszystkie głębie rzeki. Wtedy pycha Asyrii będzie poniżona, a berło Egiptu zniknie.
12 Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova ndipo adzayenda mʼdzina lake,” akutero Yehova.
Umocnię ich też w PANU i będą chodzić w jego imię, mówi PAN.

< Zekariya 10 >