< Zekariya 10 >

1 Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira; ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula. Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu, ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
Celani eNkosini izulu ngesikhathi sezulu langemuva; iNkosi yenza imibane, ibanike izihlambo zezulu, kulolo lalolo uhlaza egangeni.
2 Mafano amayankhula zachinyengo, owombeza mawula amaona masomphenya abodza; amafotokoza maloto onama, amapereka chitonthozo chopandapake. Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika chifukwa chosowa mʼbusa.
Ngoba izithombe zikhulume ize, labavumisi babone amanga, balandisa amaphupho ayinkohliso, baduduza ngokuyize. Ngakho-ke bazihambela njengezimvu, badubeka, ngoba kwakungelamelusi.
3 “Ine ndawakwiyira kwambiri abusa, ndipo ndidzalanga atsogoleri; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira nkhosa zake, nyumba ya Yuda, ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
Intukuthelo yami yavutha imelene labelusi, ngajezisa izimpongo; ngoba iNkosi yamabandla izawuhambela umhlambi wayo, indlu kaJuda; ibenze babe njengebhiza layo elihlekazi empini.
4 Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya, mudzachokera chikhomo cha tenti, mudzachokera uta wankhondo, mudzachokera mtsogoleri aliyense.
Kwaphuma kuye igumbi, kuye isikhonkwane, kuye idandili lempi, kuye wonke umcindezeli ndawonye.
5 Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo. Chifukwa Yehova adzakhala nawo, adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.
Futhi bazakuba njengamaqhawe anyathela odakeni lwezitalada empini; njalo bazakulwa, ngoba iNkosi ilabo, bayangise abagadi bamabhiza.
6 “Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe. Ndidzawabwezeretsa chifukwa ndawamvera chisoni. Adzakhala ngati kuti sindinawakane, chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.
Njalo ngizaqinisa indlu kaJuda, ngisindise indlu kaJosefa, ngibabuyise, ngoba ngilesihawu kubo. Njalo bazakuba njengokungathi kangizanga ngibalahle; ngoba ngiyiNkosi uNkulunkulu wabo, ngibezwe.
7 Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo. Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala; mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
Njalo amaEfrayimi azakuba njengeqhawe, lenhliziyo yawo ithokoze njengangewayini. Yebo abantwana bawo bazakubona, bathokoze; inhliziyo yawo izathokoza eNkosini.
8 Ndidzaliza mluzu ndi kuwasonkhanitsa pamodzi. Ndithu ndawawombola; adzachulukana ngati poyamba paja.
Ngizabatshayela ukhwelo, ngibabuthe; ngoba ngibahlengile; njalo bazakwanda njengoba sebandile.
9 Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu, koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira. Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka, ndipo adzabwerera.
Njalo ngizabahlanyela phakathi kwezizwe, bangikhumbule endaweni ezikhatshana; baphile labantwana babo, baphenduke.
10 Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya. Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni, mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
Ngibabuyise bevela elizweni leGibhithe, ngibaqoqe baphume eAsiriya; ngibalethe elizweni leGileyadi leLebhanoni, kodwa kabayikutholelwa ndawo.
11 Adzawoloka nyanja ya masautso; nyanja yokokoma idzagonja ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa. Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
Njalo uzadabula olwandle lenhlupheko, atshaye amagagasi olwandle, lazo zonke izinziki zomfula zizakoma; lokuzigqaja kweAsiriya kwehliswe, lentonga yobukhosi yeGibhithe isuke.
12 Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova ndipo adzayenda mʼdzina lake,” akutero Yehova.
Njalo ngizabaqinisa eNkosini; bahambe besiya le lale ebizweni layo, itsho iNkosi.

< Zekariya 10 >