< Zekariya 10 >

1 Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira; ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula. Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu, ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
Demandez à Yahweh de la pluie au printemps. C’est Yahweh qui fait les éclairs; il leur donnera une pluie abondante, à chacun de l’herbe dans son champ.
2 Mafano amayankhula zachinyengo, owombeza mawula amaona masomphenya abodza; amafotokoza maloto onama, amapereka chitonthozo chopandapake. Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika chifukwa chosowa mʼbusa.
Car les théraphim ont parlé futilité, et les devins ont eu des visions de mensonge; ils débitent de vains songes, et donnent de fausses consolations. C’est pourquoi ils sont partis comme un troupeau; ils ont été opprimés, faute de berger.
3 “Ine ndawakwiyira kwambiri abusa, ndipo ndidzalanga atsogoleri; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira nkhosa zake, nyumba ya Yuda, ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
Ma colère s’est enflammée contre les bergers, et je châtierai les boucs! Car Yahweh des armées visite son troupeau, la maison de Juda, et il en fait son cheval d’honneur dans la bataille.
4 Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya, mudzachokera chikhomo cha tenti, mudzachokera uta wankhondo, mudzachokera mtsogoleri aliyense.
De lui viendra la troupe, de lui le pieu, de lui l’arc de guerre; de lui sortiront tous les chefs ensemble.
5 Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo. Chifukwa Yehova adzakhala nawo, adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.
Ils seront comme des héros, foulant la boue des chemins dans la bataille; ils combattront, car Yahweh sera avec eux, et ils couvriront de honte ceux qui sont montés sur des chevaux.
6 “Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe. Ndidzawabwezeretsa chifukwa ndawamvera chisoni. Adzakhala ngati kuti sindinawakane, chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.
Je fortifierai la maison de Juda, et je sauverai la maison de Joseph; je les rétablirai, car j’ai compassion d’eux, et ils seront comme si je ne les avais pas rejetés. Car moi, je suis Yahweh, leur Dieu, et je les exaucerai.
7 Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo. Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala; mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
Ceux d’Ephraïm seront comme des héros, et leur cœur sera joyeux comme par le vin; leurs fils le verront et se réjouiront, et leur cœur tressaillira en Yahweh.
8 Ndidzaliza mluzu ndi kuwasonkhanitsa pamodzi. Ndithu ndawawombola; adzachulukana ngati poyamba paja.
Je sifflerai après eux, et je les rassemblerai, car je les ai rachetés, et ils se multiplieront comme ils s’étaient multipliés.
9 Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu, koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira. Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka, ndipo adzabwerera.
Quand je les aurai répandus parmi les peuples, et qu’ils se souviendront de moi dans les pays lointains, ils vivront avec leurs enfants et ils reviendront.
10 Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya. Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni, mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
Je les ramènerai du pays d’Égypte, et je les rassemblerai d’Assyrie, et je les ferai venir au pays de Galaad et au Liban, et il ne se trouvera pas assez d’espace pour eux.
11 Adzawoloka nyanja ya masautso; nyanja yokokoma idzagonja ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa. Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
Il passera par la mer, mer de détresse, il frappera les flots dans la mer, et toutes les profondeurs du fleuve seront mises à sec. L’orgueil de l’Assyrie sera abattu, et le sceptre de l’Égypte sera ôté.
12 Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova ndipo adzayenda mʼdzina lake,” akutero Yehova.
Je les fortifierai en Yahweh, et ils marcheront en son nom, — oracle de Yahweh.

< Zekariya 10 >