< Tito 1 >
1 Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu
Milý Tite, můj duchovní synu, jsem poslán hlásat víru těm, které si Bůh vyvolil, učit je poznávat Boží pravdy, které proměňují život.
2 ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios )
Kdo je přijme, získá nehynoucí život, (aiōnios )
3 Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.
slíbený od Boha již před dávnými věky. Nyní Bůh svůj slib Kristovým prostřednictvím potvrdil a po celém světě rozhlašuje zprávu o věčném životě. Z jeho příkazu jsem i já byl pověřen účastí na tomto díle.
4 Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.
Přeji ti, můj synu, aby tě Bůh Otec i Ježíš Kristus, náš Zachránce, obdařil svým pokojem a milostí.
5 Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira.
Nechal jsem tě na Krétě, abys tam uvedl do pořádku, co jsem já už nestihl, a abys podle mých pokynů ustanovil v každém městě starší.
6 Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera.
Připomínám: musí to být muži bezvadné pověsti, jen jednou ženatí, též jejich děti musí být oddány Ježíši Kristu, své rodiče musí mít v úctě a nepohoršovat svou nezvedeností.
7 Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo.
Církevní představený je přece Boží správce, a proto musí být mužem bezúhonným: ani domýšlivec, ani vztekloun, ani pijan, ani rváč, ani ziskuchtivý.
8 Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo.
Musí být pohostinný, dobrosrdečný, rozvážný, nestranný, zbožný a zdrženlivý.
9 Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.
Jeho život musí být v dokonalém souladu s vírou, kterou hlásá, aby měl právo nabádat k zdravému učení a umlčovat odpůrce.
10 Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo.
Je totiž spousta těch, kteří tvrdohlavě překrucují pravdu, hlavně mezi bývalými židy.
11 Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo.
Těm je třeba zavřít ústa. Do mnoha rodin vnesli zmatek, a to jen proto, aby mohli lovit v kalných vodách.
12 Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.”
Konečně sám jeden z nich, považovaný dokonce za proroka, charakterizoval své krajany takto: „Kréťané jsou lháři, dobytek a břicha lenivá.“
13 Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona,
Opravdu výstižné! Buď na ně co nejpřísnější, aby konečně dostali rozum a přišli ke správné víře.
14 kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi.
Vždyť ty židovské báje a vymyšlené předpisy zatemňují pravdu.
15 Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa.
Kdo má čisté srdce, tomu se všechno jeví dobré a čisté. Ale kdo je uvnitř zlý a bezbožný, nachází totéž i kolem sebe, protože se na svět dívá brýlemi svého vlastního špinavého nitra.
16 Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.
Takové osoby prohlašují, že znají Boha, ale způsob jejich jednání je usvědčuje ze lži. Jsou protivní, zpupní a neschopní dobrého skutku.