< Tito 3 >

1 Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino.
Opominji ih da budu pokorni i poslušni gospodarima i zapovjednicima, i gotovi na svako dobro djelo;
2 Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.
Ni na koga da ne hule, da se ne svaðaju, nego da budu mirni, svaku krotost da pokazuju svijem ljudima,
3 Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake.
Jer i mi bijasmo negda ludi, i nepokorni, i prevareni, služeæi razliènijem željama i slastima, u pakosti i zavisti živeæi, mrski buduæi i mrzeæi jedan na drugoga.
4 Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera,
A kad se pokaza blagodat i èovjekoljublje spasa našega Boga,
5 Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera
Ne za djela pravedna koja mi uèinismo, nego po svojoj milosti spase nas banjom preroðenja i obnovljenjem Duha svetoga,
6 amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu,
Kojega izli na nas obilno kroz Isusa Hrista spasitelja našega,
7 kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. (aiōnios g166)
Da se opravdamo blagodaæu njegovom, i da budemo našljednici života vjeènoga po nadu. (aiōnios g166)
8 Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.
Sine Tite! istinita je rijeè, i u ovome hoæu da utvrðuješ, da se oni koji vjerovaše Bogu trude i staraju za dobro djelo: ovo je korisno ljudima i dobro.
9 Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake.
A ludijeh zapitkivanja i teftera od plemena, i svaða i prepiranja o zakonu kloni se; jer je to nekorisno i prazno.
10 Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe.
Èovjeka jeretika po prvome i drugom svjetovanju kloni se,
11 Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.
Znajuæi da se takovi izopaèio, i griješi, i sam je sebe osudio.
12 Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira.
Kad pošljem k tebi Artemu ili Tihika, postaraj se da doðeš k meni u Nikopolj, jer sam namislio da ondje zimujem.
13 Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu.
Zinu zakonika i Apola lijepo opremi da imaju sve što im treba.
14 Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.
Ali i naši neka se uèe napredovati u dobrijem djelima, ako gdje bude od potrebe da ne budu bez roda.
15 Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro. Chisomo chikhale ndi inu nonse.
Pozdravljaju te svi koji su sa mnom. Pozdravi sve koji nas ljube u vjeri. Blagodat sa svima vama. Amin.

< Tito 3 >