< Tito 3 >
1 Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino.
Admonish them to be submissive to governors and magistrates, to obey their orders, and to be ready to every good work;
2 Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.
to slander no man, to avoid contention, to be gentle, shewing all meekness unto all men.
3 Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake.
For we also were formerly foolish, disobedient, going astray, enslaved to various disorderly appetites and pleasures, living in malice and envy, hateful, and hating one another.
4 Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera,
But when the kindness and love of God our Saviour towards man appeared,
5 Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera
not for works of righteousness which we had done, but according to his own mercy He saved us, by the washing of regeneration, and renewing of the holy Spirit;
6 amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu,
which He hath plentifully shed upon us, through Jesus Christ our Saviour:
7 kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. (aiōnios )
that being justified by his grace, we might become heirs according to the hope of eternal life. (aiōnios )
8 Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.
This is a word which ought to believed and observed, and concerning these things I would have thee stedfastly affirm, that they who have believed in God be careful to excel in good works: for these things are good and profitable to men.
9 Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake.
But avoid foolish questions, and genealogies, and strifes and contentions about the law; for they are unprofitable and vain:
10 Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe.
reject therefore such an heretical man, after the first and second admonition; knowing that such a one is perverted,
11 Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.
and sinneth as being self-condemned.
12 Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira.
When I shall send Artemas to thee, or Tychicus, endeavour to come to me to Nicopolis: for there I have determined to winter.
13 Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu.
Forward Zenas the lawyer, and Apollos, on their journey carefully, that nothing may be wanting to them.
14 Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.
And let our brethren-also learn to excel in good works for necessary exigencies, that they may not be unfruitful.
15 Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro. Chisomo chikhale ndi inu nonse.
All that are with me salute thee. Salute them that love us in the faith. Grace be with you all. Amen.