< Tito 3 >

1 Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino.
Remind them to be in subjection to rulers and to authorities, to be obedient, to be ready for every good work,
2 Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.
to speak evil of no one, not to be contentious, to be gentle, showing courtesy to all people.
3 Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake.
For we were also once foolish, disobedient, deceived, serving various lusts and pleasures, living in malice and envy, hateful, and hating one another.
4 Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera,
But when the kindness of God our Savior and his love toward humankind appeared,
5 Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera
not by works of righteousness, which we did ourselves, but according to his mercy, he saved us, through the washing of rebirth and renewing by the Rukha d'Qudsha,
6 amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu,
whom he poured out on us richly, through Yeshua Meshikha our Savior;
7 kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. (aiōnios g166)
that, being justified by his grace, we might be made heirs according to the hope of everlasting life. (aiōnios g166)
8 Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.
This saying is faithful, and concerning these things I desire that you affirm confidently, so that those who have believed God may be careful to maintain good works. These things are good and profitable for people;
9 Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake.
but shun foolish questionings, genealogies, strife, and disputes about the law; for they are unprofitable and vain.
10 Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe.
Reject a divisive person after a first and second warning;
11 Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.
knowing that such a one is perverted, and sins, being self-condemned.
12 Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira.
When I send Artemas to you, or Tychicus, be diligent to come to me to Nicopolis, for I have determined to winter there.
13 Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu.
Send Zenas, the Law scholar, and Apollos on their journey speedily, that nothing may be lacking for them.
14 Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.
Let our people also learn to maintain good works for necessary uses, that they may not be unfruitful.
15 Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro. Chisomo chikhale ndi inu nonse.
All who are with me greet you. Greet those who love us in faith. Grace be with you all.

< Tito 3 >