< Tito 3 >

1 Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino.
Lizinong nani i ne ati bara anan tigo nin nanan tica tig, inunku vat.
2 Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.
Na iwa firin umong b, na iwa su mayerdan ba na isun anit ti bau mine nin dursuzu nteltinu nati udu na ti vat
3 Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake.
Bara nani arik atibite nwa di sa ukpilzu nin salin nunku nat, tiwa cinu hem ti so acin kuna niyizi nin lanzun mman. Tiwa di nanyan likara linanzan nnin shina. Tiwa nari ati bite nin salin laun mmang.
4 Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera,
Bara na nshau kibinai Kutelle unan tucu bite nin son suu me udu kitin nit adaa.
5 Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera
Awa tucu nari nnuzun maru upese nin lipesen Nfip mi la, na bara ni tawaa na tisuzu b, bara nani nkunekune mer.
6 amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu,
Kutelle na ni nari Nfip me milau nanya Yesu kristi unan tucu bite.
7 kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. (aiōnios g166)
Awa suu nani tina see usortu nanya mbolu Kutell, ti da su anan lin gadu nlai sa ligang nin likara kibinai. (aiōnios g166)
8 Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.
Too ti pipinghe tinyinuwari. Ndi nin suu iliru nin likara kibinai bara ele imon, ara ale na uyinna nin Kutelle iceu nibinai mine nitwa ni cine naa ana ceu nbugn min. I le imone caun nin se ugb ardan bara anit vat.
9 Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake.
Bara nani sunan mayardan tilalalng tone nin piziru na kura nin fizu nibinai nnun bara uduk. I leli imone na icau ba nin salin nimong kitene.
10 Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe.
Nari ule na adin dasu nin kosu natii nanya mine iwa malu wunughe atuf urun sa tiba.
11 Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.
Nin yinu au umusin ntele amlu killau liti me nanya libau ti terd nin tizu kulapi nca nkul.
12 Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira.
Dana iwa tuu Artamas sa Tychikus ku kiti mine tanmas idak kiti nighe in Nikopolis kikaa nan ina yinin in soo ku kubin tutuwui.
13 Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu.
Tanmas ituu Zinas ku unan yiru ndoka. nin Apollo, nin nimong ile na idinin suwe.
14 Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.
Na amit bite masu nitwa nicine nanga na nima bizu ti bukata ti kpaikpai bara iwa so sa nitwa ba
15 Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro. Chisomo chikhale ndi inu nonse.
Vat nale na idi nin me idin lisu min. Lison ale na idi ni su bite nanya yinnu sa uyenu ubolu Kutelle soo nan ghin. usuo nani

< Tito 3 >