< Tito 2 >

1 Koma iwe uziphunzitsa zogwirizana ndi chiphunzitso choona.
Men tal du det som sømmer sig for den sunde lære,
2 Phunzitsa amuna achikulire kuti akhale osaledzera, aulemu wawo, odziletsa, okhwima mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkupirira.
at gamle menn skal være edrue, verdige, sindige, sunde i troen, i kjærligheten, i tålmodet;
3 Chimodzimodzinso, phunzitsa amayi achikulire kuti akhale aulemu mʼmakhalidwe awo, asakhale osinjirira anzawo kapena zidakwa, koma akhale alangizi abwino.
likeså at gamle kvinner i sin ferd skal te sig som det sømmer sig for hellige, ikke fare med baktalelse, ikke være træler av drikk, men veiledere i det gode,
4 Tsono atha kulangiza amayi achichepere kukonda amuna awo ndi ana awo.
forat de kan lære de unge kvinner å elske sine menn og sine barn,
5 Kuwaphunzitsa kukhala odziletsa ndi oyera mtima, osamala bwino mabanja awo, okoma mtima, ndi ogonjera amuna awo. Choncho palibe amene adzanyoze mawu a Mulungu.
å være sindige, rene, huslige, gode, lydige mot sine egne menn, forat Guds ord ikke skal bli spottet!
6 Momwemonso, uwalimbikitse amuna achichepere kuti akhale odziletsa.
De unge menn skal du likeledes formane til å være sindige,
7 Pa zonse iwe mwini ukhale chitsanzo pa ntchito zabwino. Pa chiphunzitso chako uwonetsa kuona mtima ndi kutsimikiza mtima kwako.
idet du i alle måter ter dig selv som et forbillede i gode gjerninger, og i din lære viser renhet, verdighet,
8 Phunzitsa choonadi kuti anthu asapeze chokutsutsa, motero wotsutsana nawe adzachita manyazi chifukwa adzasowa kanthu koyipa kuti atinenere.
en sund, ulastelig tale, forat motstanderen må gå i sig selv, idet han ikke har noget ondt å si om oss.
9 Phunzitsa akapolo kuti azigonjera ambuye awo mu zinthu zonse ndi kuwakondweretsa. Asamatsutsane nawo
Tjenere skal du formane til å være lydige mot sine egne herrer, i alle ting å tekkes dem, ikke å si imot,
10 kapena kumawabera, koma adzionetse kuti ndi odalirika, motero pa zochita zawo zonse adzaonetsa ubwino wa chiphunzitso cha Mulungu, Mpulumutsi wathu.
ikke å være utro, men vise all god troskap, forat de i alt kan være en pryd for Guds, vår frelsers lære.
11 Pakuti chisomo cha Mulungu chimene chimapulumutsa chaonekera kwa anthu onse.
For Guds nåde er åpenbaret til frelse for alle mennesker,
12 Chisomo chimatiphunzitsa kukana moyo osalemekeza Mulungu komanso zilakolako za dziko lapansi. Ndipo chimatiphunzitsa kukhala moyo odziletsa, olungama ndi opembedza Mulungu nthawi ino, (aiōn g165)
idet den optukter oss til å fornekte ugudelighet og de verdslige lyster og leve tuktig og rettferdig og gudfryktig i den nuværende verden, (aiōn g165)
13 pamene tikudikira chiyembekezo chodala; kuonekera kwa ulemerero wa Mulungu wathu wamkulu ndi Mpulumutsi, Yesu Khristu,
mens vi venter på det salige håp og åpenbarelsen av den store Guds og vår frelser Jesu Kristi herlighet,
14 amene anadzipereka yekha chifukwa cha ife kutiwombola ku zoyipa zonse ndi kudziyeretsera yekha anthu amene ndi akeake, achangu pa ntchito yabwino.
han som gav sig selv for oss for å forløse oss fra all urettferdighet og rense sig selv et eiendomsfolk, nidkjært til gode gjerninger.
15 Tsono zimenezi ndi zinthu zomwe uyenera kuphunzitsa. Uziwalimbikitsa anthu ndi kuwatsutsa komwe. Uzichita zimenezi ndi ulamuliro wonse. Wina aliyense asakupeputse ayi.
Tal dette og forman og irettesett med all myndighet! La ingen ringeakte dig!

< Tito 2 >