< Tito 2 >

1 Koma iwe uziphunzitsa zogwirizana ndi chiphunzitso choona.
But speak thou the things which befit the sound doctrine:
2 Phunzitsa amuna achikulire kuti akhale osaledzera, aulemu wawo, odziletsa, okhwima mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkupirira.
that aged men be temperate, grave, sober-minded, sound in faith, in love, in patience:
3 Chimodzimodzinso, phunzitsa amayi achikulire kuti akhale aulemu mʼmakhalidwe awo, asakhale osinjirira anzawo kapena zidakwa, koma akhale alangizi abwino.
that aged women likewise be reverent in demeanor, not slanderers nor enslaved to much wine, teachers of that which is good;
4 Tsono atha kulangiza amayi achichepere kukonda amuna awo ndi ana awo.
that they may train the young women to love their husbands, to love their children,
5 Kuwaphunzitsa kukhala odziletsa ndi oyera mtima, osamala bwino mabanja awo, okoma mtima, ndi ogonjera amuna awo. Choncho palibe amene adzanyoze mawu a Mulungu.
[to be] sober-minded, chaste, workers at home, kind, being in subjection to their own husbands, that the word of God be not blasphemed:
6 Momwemonso, uwalimbikitse amuna achichepere kuti akhale odziletsa.
the younger men likewise exhort to be sober-minded:
7 Pa zonse iwe mwini ukhale chitsanzo pa ntchito zabwino. Pa chiphunzitso chako uwonetsa kuona mtima ndi kutsimikiza mtima kwako.
in all things showing thyself an ensample of good works; in thy doctrine [showing] uncorruptness, gravity,
8 Phunzitsa choonadi kuti anthu asapeze chokutsutsa, motero wotsutsana nawe adzachita manyazi chifukwa adzasowa kanthu koyipa kuti atinenere.
sound speech, that cannot be condemned; that he that is of the contrary part may be ashamed, having no evil thing to say of us.
9 Phunzitsa akapolo kuti azigonjera ambuye awo mu zinthu zonse ndi kuwakondweretsa. Asamatsutsane nawo
[Exhort] servants to be in subjection to their own masters, [and] to be well-pleasing [to them] in all things; not gainsaying;
10 kapena kumawabera, koma adzionetse kuti ndi odalirika, motero pa zochita zawo zonse adzaonetsa ubwino wa chiphunzitso cha Mulungu, Mpulumutsi wathu.
not purloining, but showing all good fidelity; that they may adorn the doctrine of God our Saviour in all things.
11 Pakuti chisomo cha Mulungu chimene chimapulumutsa chaonekera kwa anthu onse.
For the grace of God hath appeared, bringing salvation to all men,
12 Chisomo chimatiphunzitsa kukana moyo osalemekeza Mulungu komanso zilakolako za dziko lapansi. Ndipo chimatiphunzitsa kukhala moyo odziletsa, olungama ndi opembedza Mulungu nthawi ino, (aiōn g165)
instructing us, to the intent that, denying ungodliness and worldly lusts, we should live soberly and righteously and godly in this present world; (aiōn g165)
13 pamene tikudikira chiyembekezo chodala; kuonekera kwa ulemerero wa Mulungu wathu wamkulu ndi Mpulumutsi, Yesu Khristu,
looking for the blessed hope and appearing of the glory of the great God and our Saviour Jesus Christ;
14 amene anadzipereka yekha chifukwa cha ife kutiwombola ku zoyipa zonse ndi kudziyeretsera yekha anthu amene ndi akeake, achangu pa ntchito yabwino.
who gave himself for us, that he might redeem us from all iniquity, and purify unto himself a people for his own possession, zealous of good works.
15 Tsono zimenezi ndi zinthu zomwe uyenera kuphunzitsa. Uziwalimbikitsa anthu ndi kuwatsutsa komwe. Uzichita zimenezi ndi ulamuliro wonse. Wina aliyense asakupeputse ayi.
These things speak and exhort and reprove with all authority. Let no man despise thee.

< Tito 2 >