< Tito 1 >
1 Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu
Paulus, Guds tjänare och Jesu Kristi apostel, sänd att verka för Guds utvaldas tro och för kunskapen om den sanning som hör gudsfruktan till,
2 ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios )
sänd, därför att det finnes ett hopp om evigt liv -- ty evigt liv har Gud, som icke kan ljuga, för evärdliga tider sedan utlovat, (aiōnios )
3 Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.
och när tiden var inne, uppenbarade han sitt ord i den predikan varmed jag genom Guds, vår Frälsares, befallning blev betrodd --
4 Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.
jag, Paulus, hälsar Titus, min sannskyldige son på grund av gemensam tro. Nåd och frid ifrån Gud, Fadern, och Kristus Jesus, vår Frälsare!
5 Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira.
När jag lämnade dig kvar på Kreta, var det för att du skulle ordna vad som ännu återstod att ordna, och för att du, på det sätt som jag har ålagt dig, skulle i var särskild stad tillsätta äldste,
6 Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera.
varhelst någon oförvitlig man funnes, en enda kvinnas man, en som hade troende barn, vilka icke vore i vanrykte för oskickligt leverne eller vore uppstudsiga.
7 Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo.
Ty en församlingsföreståndare bör vara oförvitlig, såsom det höves en Guds förvaltare, icke självgod, icke snar till vrede, icke begiven på vin, icke våldsam, icke sniken efter slem vinning.
8 Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo.
Han bör fastmer vara gästvänlig, nitälska för vad gott är, leva tuktigt, rättfärdigt, heligt och återhållsamt;
9 Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.
han bör hålla sig stadigt vid det fasta ordet, såsom han har fått lära det, så att han är mäktig både att förmana medelst den sunda läran och att vederlägga dem som säga emot.
10 Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo.
Ty många finnas som icke vilja veta av någon myndighet, många som föra fåfängligt tal och bedraga människors sinnen; så göra i synnerhet de omskurna.
11 Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo.
På sådana bör man tysta munnen, ty de förvilla hela hus genom att för slem vinnings skull förkunna otillbörliga läror.
12 Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.”
En av dem, en profet av deras eget folk, har sagt: »Kreterna, lögnare jämt, äro odjur, glupska och lata.»
13 Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona,
Och det vittnesbördet är sant. Du skall därför strängt tillrättavisa dem, så att de bliva sunda i tron
14 kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi.
och icke akta på judiska fabler och vad som påbjudes av människor som vända sig från sanningen.
15 Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa.
Allt är rent för dem som äro rena; men för de orena och otrogna är intet rent, utan hos dem äro både förstånd och samvete orenade.
16 Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.
De säga sig känna Gud, men med sina gärningar förneka de det; ty de äro vederstyggliga och ohörsamma människor, odugliga till allt gott verk.