< Tito 1 >

1 Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu
anantajīvanasyāśātō jātāyā īśvarabhaktē ryōgyasya satyamatasya yat tatvajñānaṁ yaśca viśvāsa īśvarasyābhirucitalōkai rlabhyatē tadarthaṁ (aiōnios g166)
2 ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios g166)
yīśukhrīṣṭasya prērita īśvarasya dāsaḥ paulō'haṁ sādhāraṇaviśvāsāt mama prakr̥taṁ dharmmaputraṁ tītaṁ prati likhami|
3 Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.
niṣkapaṭa īśvara ādikālāt pūrvvaṁ tat jīvanaṁ pratijñātavān svanirūpitasamayē ca ghōṣaṇayā tat prakāśitavān|
4 Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.
mama trāturīśvarasyājñayā ca tasya ghōṣaṇaṁ mayi samarpitam abhūt| asmākaṁ tāta īśvaraḥ paritrātā prabhu ryīśukhrīṣṭaśca tubhyam anugrahaṁ dayāṁ śāntiñca vitaratu|
5 Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira.
tvaṁ yad asampūrṇakāryyāṇi sampūrayē rmadīyādēśācca pratinagaraṁ prācīnagaṇān niyōjayēstadarthamahaṁ tvāṁ krītyupadvīpē sthāpayitvā gatavān|
6 Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera.
tasmād yō narō 'nindita ēkasyā yōṣitaḥ svāmī viśvāsinām apacayasyāvādhyatvasya vā dōṣēṇāliptānāñca santānānāṁ janakō bhavati sa ēva yōgyaḥ|
7 Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo.
yatō hētōradyakṣēṇēśvarasya gr̥hādyakṣēṇēvānindanīyēna bhavitavyaṁ| tēna svēcchācāriṇā krōdhinā pānāsaktēna prahārakēṇa lōbhinā vā na bhavitavyaṁ
8 Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo.
kintvatithisēvakēna sallōkānurāgiṇā vinītēna nyāyyēna dhārmmikēṇa jitēndriyēṇa ca bhavitavyaṁ,
9 Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.
upadēśē ca viśvastaṁ vākyaṁ tēna dhāritavyaṁ yataḥ sa yad yathārthēnōpadēśēna lōkān vinētuṁ vighnakāriṇaśca niruttarān karttuṁ śaknuyāt tad āvaśyakaṁ|
10 Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo.
yatastē bahavō 'vādhyā anarthakavākyavādinaḥ pravañcakāśca santi viśēṣataśchinnatvacāṁ madhyē kēcit tādr̥śā lōkāḥ santi|
11 Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo.
tēṣāñca vāgrōdha āvaśyakō yatastē kutsitalābhasyāśayānucitāni vākyāni śikṣayantō nikhilaparivārāṇāṁ sumatiṁ nāśayanti|
12 Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.”
tēṣāṁ svadēśīya ēkō bhaviṣyadvādī vacanamidamuktavān, yathā, krītīyamānavāḥ sarvvē sadā kāpaṭyavādinaḥ| hiṁsrajantusamānāstē 'lasāścōdarabhārataḥ||
13 Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona,
sākṣyamētat tathyaṁ, atō hētōstvaṁ tān gāḍhaṁ bhartsaya tē ca yathā viśvāsē svasthā bhavēyu
14 kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi.
ryihūdīyōpākhyānēṣu satyamatabhraṣṭānāṁ mānavānām ājñāsu ca manāṁsi na nivēśayēyustathādiśa|
15 Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa.
śucīnāṁ kr̥tē sarvvāṇyēva śucīni bhavanti kintu kalaṅkitānām aviśvāsināñca kr̥tē śuci kimapi na bhavati yatastēṣāṁ buddhayaḥ saṁvēdāśca kalaṅkitāḥ santi|
16 Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.
īśvarasya jñānaṁ tē pratijānanti kintu karmmabhistad anaṅgīkurvvatē yatastē garhitā anājñāgrāhiṇaḥ sarvvasatkarmmaṇaścāyōgyāḥ santi|

< Tito 1 >