< Tito 1 >

1 Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu
Pavel, slujitor al lui Dumnezeu și apostol al lui Isus Hristos, după credința celor aleși de Dumnezeu și după cunoștința adevărului, care este potrivit cu evlavia,
2 ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios g166)
în speranța vieții veșnice, pe care Dumnezeu, care nu poate minți, a făgăduit-o înainte de începutul veacurilor, (aiōnios g166)
3 Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.
dar care, la vremea Sa, a descoperit cuvântul Său în mesajul care mi-a fost încredințat, potrivit poruncii lui Dumnezeu, Mântuitorul nostru,
4 Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.
lui Tit, adevăratul meu copil, potrivit unei credințe comune: Har, milă și pace de la Dumnezeu Tatăl și de la Domnul Isus Hristos, Mântuitorul nostru.
5 Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira.
De aceea v-am lăsat în Creta, ca să puneți în ordine ce lipsește și să rânduiți bătrâni în fiecare cetate, cum v-am poruncit eu,
6 Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera.
dacă este cineva fără vină, soț al unei singure femei, cu copii credincioși, care nu sunt acuzați de desfrânare sau de neorânduială.
7 Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo.
Pentru că supraveghetorul trebuie să fie fără vină, ca un administrator al lui Dumnezeu, să nu se mulțumească cu sine, să nu se mânie ușor, să nu fie dat la vin, să nu fie violent, să nu fie lacom la câștiguri necinstite;
8 Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo.
ci să fie dat la ospitalitate, iubitor de bine, cumpătat, corect, cinstit, sfânt, stăpân pe sine,
9 Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.
să se țină de cuvântul credincios, care este conform învățăturii, ca să poată îndemna în doctrina sănătoasă și să convingă pe cei care îl contrazic.
10 Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo.
Căci sunt și mulți oameni nechibzuiți, vorbitori și înșelători, mai ales cei din circumcizie,
11 Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo.
cărora trebuie să li se astupe gura, oameni care răstălmăcesc case întregi, învățând lucruri pe care nu trebuie să le facă, pentru un câștig necinstit.
12 Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.”
Unul dintre ei, un profet de-al lor, a spus: “Creștinele sunt întotdeauna mincinoase, fiare rele și lăcomi leneși”.
13 Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona,
Această mărturie este adevărată. De aceea, mustrați-i aspru, ca să fie sănătoși în credință,
14 kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi.
fără să fie atenți la fabulațiile iudaice și la poruncile oamenilor care se îndepărtează de adevăr.
15 Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa.
Pentru cei curați, toate lucrurile sunt pure, dar pentru cei necurați și necredincioși, nimic nu este curat, ci atât mintea lor, cât și conștiința lor sunt spurcate.
16 Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.
Ei mărturisesc că îl cunosc pe Dumnezeu, dar prin faptele lor îl neagă, fiind abominabili, neascultători și nepotriviți pentru orice lucrare bună.

< Tito 1 >