< Tito 1 >

1 Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu
Paul slave God apostle then Jesus Christ according to faith select God and knowledge truth the/this/who according to piety
2 ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios g166)
upon/to/against hope life eternal which to profess the/this/who not a liar God before time eternal (aiōnios g166)
3 Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.
to reveal then time/right time one's own/private the/this/who word it/s/he in/on/among preaching which to trust (in) I/we according to command the/this/who savior me God
4 Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.
Titus genuine child according to common: shared faith grace (and *N(K)O*) peace away from God father and (lord: God *K*) Christ Jesus the/this/who savior me
5 Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira.
this/he/she/it because of (to leave *N(k)(o)*) you in/on/among Crete in order that/to the/this/who to lack to straighten out and to appoint/conduct according to city elder: Elder as/when I/we you to direct
6 Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera.
if which? to be irreproachable one woman: wife man: husband child to have/be faithful not in/on/among accusation debauchery or insubordinate
7 Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo.
be necessary for the/this/who overseer irreproachable to exist as/when God manager not self-willed not quick-tempered not drunken not bully not greedy
8 Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo.
but hospitable lover of good self-controlled just sacred self-controlled
9 Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.
to cling to the/this/who according to the/this/who teaching faithful word in order that/to able to be and to plead/comfort in/on/among the/this/who teaching the/this/who be healthy and the/this/who to dispute to rebuke
10 Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo.
to be for much and insubordinate babbler and deceiver especially the/this/who out from (the/this/who *no*) circumcision
11 Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo.
which be necessary to silence who/which all house: household to overturn to teach which not be necessary shameful gain because of
12 Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.”
to say one out from it/s/he one's own/private it/s/he prophet Cretan always liar evil/harm: evil wild animal belly idle
13 Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona,
the/this/who testimony this/he/she/it to be true through/because of which cause/charge to rebuke it/s/he severely in order that/to be healthy in/on/among the/this/who faith
14 kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi.
not to watch out Jewish myth and commandment a human to turn away the/this/who truth
15 Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa.
all (on the other hand *k*) clean the/this/who clean the/this/who then to stain and unbelieving none clean but to stain it/s/he and the/this/who mind and the/this/who conscience
16 Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.
God to confess/profess to know the/this/who then work to deny abominable to be and disobedient and to/with all work good failing

< Tito 1 >