< Tito 1 >

1 Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu
Ik'i guutsonat Iyesus Krstos wosheets wottso P'awulosoke, Ik'o galbdek'ts ashuwotsi bo imnetiyon kup'shr, Ik'i ash beyo maants jishit aro bodanetwok'o wosheetso,
2 ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios g166)
Imnetiyanúwere Ik'o dúre dúri beyo imosh noosh b́jangitsatse need'ke, koorawo Izar Izewer kashan noosh imosh jam dúroniyere shin noosh taarre. (aiōnios g166)
3 Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.
Ari b́ gizewo b́ bodtsok'on noon worits Ik'o azaztsok'on taa t shishiyitwok'o taash imets adarok'on Ik'o bí aap'tso b́ jangi.
4 Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.
Noshir wotts imnetiyon arikon t naayi wottsosh neesh Titosh, Ik'o nihoknat noon kashitso Krstos Iyesusokere s'aatonat jeenon neesh wotowe.
5 Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira.
Neen K'ert'esitse k'aztk'rtso eegoshe manutseraawo manutsir, neen tiazaztsok'on Ik'i máá eenashwotsi kit kitotse nnaashitwok'owe.
6 Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera.
Ik'i máá eenasho eeg eeg bíatse deshawonat mááts iku kenihi wottsoni, shiraats jintsi wotonat bo alek'azeyatse tuutson k'ooreraw amants nana'úwotsi detsts asho woto bín geyife.
7 Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo.
Ik'i maa jishirwo Ik'i fino adaron b́ dek'tsotse bíyatse eeg eeg deshaw s'ayino woto bín geyife, mank'owore bika bako shiyawo, káári fayerawo, masherawo, fayetsi woterawo, gizosh k'awntrawo woto bín geyife.
8 Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo.
Maniyere ib dek'fo, sheeng keewo shuntso, káts wottso, kááwo, Ik'i finosh gaaletso, bítook kewdek'faltso wotowe.
9 Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.
Arik wotts dano daniwon izosh k'efirwotsshowere aani dek'o b́falitwok'o danb́dek'ts amanets aap'ats kup'de'e.
10 Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo.
Ay ashuwots, bítsnor Ayhudi jirwotsi wottswots gofami niwo shoyirwots, alerawwots, datsmec'ron ooshirwotsnat dashirwots fa'ane.
11 Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo.
Ashaanotsi s'k boetetuwok'o wosho geyife, bo jitsit oot'o daatsosh woteraw keewo danifetst maa ash asho boshek'iri.
12 Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.”
Boyitse iko, botook nebiyiwo «K'ert'es ashuwots jam aawo kootetswotsi, gond s'ootswotsi, fin biitsts maac' geenzwotsiye» etre.
13 Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona,
Gawets gawanúwere arikee, mansh eshe shod deshaw imnetiyo bodetsetwok'o ashaanotsi ayide hadowe.
14 kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi.
Ayhudi tururi shuutso bo sha'irwok'o, ariko k'efiru ashuwots tzaziwotsno bok'ewawok'o kup'shde'e hadowe.
15 Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa.
S'ayn nib detstswotssh, jam keewo s'ayine, kiimwotsnat amaneraw ashuwotsshmó s'ayin wottso eegonwor aaliye, dabnwor bonibo wotowa bomaac'o kiimwtske.
16 Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.
«Ik'o danfone» etirune, bofiinonmó jamere etetune bísha, bo wic'iknee, alerawwotsna sheeng keewo iko k'alo falawwotsiye.

< Tito 1 >