< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
Соломунова песма над песмама.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Да ме хоће пољубити пољупцем уста својих! Јер је твоја љубав боља од вина.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Мирисом су твоја уља прекрасна; име ти је уље разлито; зато те љубе девојке.
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Вуци ме, за тобом ћемо трчати; уведе ме цар у ложницу своју; радоваћемо се и веселићемо се тобом, спомињаћемо љубав твоју више него вино; прави љубе те.
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Црна сам, али сам лепа, кћери јерусалимске, као шатори кидарски, као завеси Соломунови.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Не гледајте ме што сам црна, јер ме је сунце опалило; синови матере моје расрдивши се на ме поставише ме да чувам винограде, и не чувах свој виноград, који ја имам.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Кажи ми ти, ког љуби душа моја, где пасеш, где пландујеш? Јер зашто бих лутала међу стадима другова твојих?
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
Ако не знаш, најлепша између жена, пођи трагом за стадом, и паси јариће своје покрај станова пастирских.
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
Ти си ми, драга моја, као коњи у колима Фараоновим.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Образи су твоји окићени гривнама, и грло твоје низовима.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Начинићемо ти златне гривне са шарама сребрним.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
Док је цар за столом, нард мој пушта свој мирис.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
Драги ми је мој кита смирне, која међу дојкама мојим почива.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
Драги ми је мој грозд кипров из винограда енгадских.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
Лепа ти си, драга моја, лепа ти си! Очи су ти као у голубице.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Леп ти си, драги мој, и љубак! И постеља наша зелени се.
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
Греде су нам у кућама кедрове, даске су нам јелове.

< Nyimbo ya Solomoni 1 >