< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
[the] song of The songs which [is] of Solomon.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Let him kiss me from [the] kisses of mouth his for [are] good love your more than wine.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
To odor oils your [are] good [is] oil [which] it is poured out name your there-fore young women they love you.
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Draw me after you let us run he has brought me the king chambers his let us rejoice and let us be glad in you let us bring to remembrance love your more than wine uprightness they love you.
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
[am] black I and lovely O daughters of Jerusalem like [the] tents of Kedar like [the] tent curtains of Solomon.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
May not you look at me who I [am] blackish [on] whom has looked on me the sun [the] sons of mother my they were angry with me they made me [one who] keeps the vineyards own vineyard my which [belongs] to me not I have kept.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Tell! to me [O] whom it loves self my where? will you graze where? will you make [them] lie down at noon which to why? will I be like a veiled [woman] with [the] flocks of companions your.
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
If not you know yourself O beautiful [one] among women go out yourself in [the] footprints of the flock and pasture young goats your at [the] dwelling places of the shepherds.
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
To mare my among [the] chariots of Pharaoh I liken you O friend my.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
They are beautiful cheeks your with strings of jewels neck your with strings of beads.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Necklaces of gold we will make for you with beads of silver.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
Until that the king [was] at table his nard my it gave forth odor its.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
[is] [the] bag of Myrrh - lover my to me between breasts my it lodges.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
[is] [the] cluster of Henna blossom - lover my to me in [the] vineyards of En Gedi.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
Here you [are] beautiful O friend my here you [are] beautiful eyes your [are] doves.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Here you [are] beautiful O lover my also pleasant also bed our [is] luxuriant.
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
[the] beams of Houses our [are] cedar (rafters our *Q(K)*) [are] cypress.

< Nyimbo ya Solomoni 1 >