< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
The Song of Songs, which is by Solomon.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
[[M.]] O that he would kiss me with one of the kisses of his mouth! For thy love is better than wine.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Because of the savor of thy precious perfumes, (Thy name is like fragrant oil poured forth, ) Therefore do the virgins love thee.
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Draw me after thee; let us run! The king hath led me to his chambers! We will be glad and rejoice in thee; We will praise thy love more than wine. Justly do they love thee!
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
I am black, but comely, O ye daughters of Jerusalem, As the tents of Kedar, as the curtains of Solomon.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Gaze not upon me because I am black, Because the sun hath looked upon me! My mother's sons were angry with me; They made me keeper of the vineyards; My vineyard, my own, have I not kept.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Tell me, thou whom my soul loveth, where thou feedest thy flock, Where thou leadest it to rest at noon; For why should I be like a veiled one by the flocks of thy companions?
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
[[Lad.]] If thou know not, O thou fairest among women, Trace thou thy way by the tracks of the flock, And feed thy kids beside the shepherds' tents!
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
[[Lov.]] To the horses in the chariots of Pharaoh Do I compare thee, my love!
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Comely are thy cheeks with rows of jewels, Thy neck with strings of pearls.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Golden chains will we make for thee, With studs of silver.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
[[M.]] While the king reclineth at his table, My spikenard sendeth forth its fragrance.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
A bunch of myrrh is my beloved to me; He shall abide between my breasts.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
My beloved is to me a cluster of henna-flowers From the gardens of Engedi.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
[[Lov.]] Behold, thou art fair, my love; behold, thou art fair! Thine eyes are doves.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
[[M.]] Behold, thou art fair, my beloved, yea, lovely; And green is our bed.
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
The cedars are the beams of our house, And its roof the cypresses.

< Nyimbo ya Solomoni 1 >