< Nyimbo ya Solomoni 1 >
1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
Salomonova Pjesma nad pjesmama
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Poljubi me poljupcem usta svojih, ljubav je tvoja slađa od vina.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Miris najboljih mirodija, ulje razlito ime je tvoje, zato te ljube djevojke.
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Povuci me za sobom, bježimo! Kralj me uveo u odaje svoje. Igrat ćemo se i radovati zbog tebe, slavit ćemo ljubav tvoju više nego vino. Pravo je da te ljube.
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Crna sam ali lijepa, kćeri jeruzalemske, kao šatori kedarski, kao zavjese Salomonove.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Ne gledajte što sam garava, to me sunce opalilo. Sinovi majke moje rasrdili se na mene, postavili me da čuvam vinograde; a svog vinograda, koji je u meni, nisam čuvala.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Reci mi, ti koga ljubi duša moja, gdje paseš, gdje se u podne odmaraš, da ne lutam, tražeći te, oko stada tvojih drugova.
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
Ako ne znaš, o najljepša među ženama, izađi i slijedi tragove stada i pasi kozliće svoje oko pastirskih koliba.
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
Usporedio bih te s konjima pod kolima faraonovim, o prijateljice moja.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Lijepi su obrazi tvoji među naušnicama, vrat tvoj pod ogrlicama.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Učinit ćemo za tebe zlatne naušnice s privjescima srebrnim.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
- Dok se kralj odmara na svojim dušecima, (tada) nard moj miriše.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
Dragi mi je moj stručak smirne što mi među grudima počiva.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
Dragi mi je moj grozd ciprov u vinogradima engedskim.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
- Gle, kako si lijepa, prijateljice moja, gle, kako si lijepa, imaš oči kao golubica.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
- Gle, kako si lijep, dragi moj, gle, kako si mio. Zelenilo je postelja naša.
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
- Grede kuća naših cedri su, a natkrovlje čempresi.