< Nyimbo ya Solomoni 8 >

1 Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga, amene anayamwa mawere a amayi anga! Ndikanakumana nawe pa njira, ndikanakupsompsona, ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.
Kaut tu būtu mans brālis, kas zīdis manas mātes krūtis? Kad es tevi atrastu ārā, es tevi skūpstītu un netaptu nicināta.
2 Ndikanakutenga ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, amayi amene anandiphunzitsa, ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe, zotsekemera za makangadza.
Es tevi vadītu, es tevi vestu savas mātes namā, ka tu mani mācītu; tad es tev dotu dzert jauktu vīnu un no savu granātābolu sulas.
3 Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.
Viņa kreisā roka ir apakš manas galvas, un viņa labā roka mani apkampj.
4 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani: musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
Es jūs mīļi lūdzu, Jeruzālemes meitas, ko jūs uztraucat un modinājāt mīlestību, pirms tai pašai patīk?
5 Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo, atatsamira wokondedwa wakeyo? Mkazi Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi, pamenepo ndi pamene amayi anachirira, pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.
Kas tā tāda, kas nāk no tuksneša un atslienas uz savu draugu? Apakš ābeles es tevi esmu uzmodinājis; tur tava māte tevi ar sāpēm ir dzemdējusi, tur sāpes ir bijušas tavai dzemdētājai.
6 Undiyike pamtima pako ngati chidindo, ngati chidindo cha pa dzanja lako; pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa, nsanje ndiyaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti lawilawi ngati malawi a moto wamphamvu. (Sheol h7585)
Liec mani kā zieģeli pie savas sirds, kā gredzenu pie savas rokas! Mīlestība ir stipra kā nāve un viņas karstums ir varens kā elle; viņas liesmas ir degošas liesmas, Dieva liesmas. (Sheol h7585)
7 Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi, mitsinje singachikokolole chikondicho. Ngati wina apereka chuma chonse cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi, adzangonyozeka nazo kotheratu.
Lieli ūdeņi mīlestību nevar apdzēst, nedz upes viņu apslīcināt. Jebšu kas visu sava nama mantu gribētu dot par mīlestību, tomēr viņš paliktu tikai par apsmieklu.
8 Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono, koma alibe mawere, kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu pa tsiku limene adzamufunsire?
Mums ir viena maza māsa, kam krūšu vēl nav, - ko mēs ar savu māsu darīsim tai dienā, kad viņu precēs?
9 Ngati iye ndi khoma, tidzamumangira nsanja ya siliva. Ngati iye ndi chitseko, tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.
Ja viņa ir mūris, tad mēs uz viņu uztaisīsim sudraba torni; ja viņa ir durvis, tad mēs tās sargāsim ar ciedru dēļiem.
10 Ine ndili ngati khoma, ndipo mawere anga ndi nsanja zake. Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa ndine wobweretsa mtendere.
Es biju mūris un manas krūtis bija kā torņi; tad es viņa acīs atradu mieru.
11 Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni; iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi, aliyense mwa iwo ankayenera kupereka ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.
Salamanam bija vīna dārzs BaālAmonā, šo vīna dārzu viņš izdeva sargiem, ikviens par viņa augļiem deva tūkstoš sudraba gabalus.
12 Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha. Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000 ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.
Mans vīna dārzs, kas man pieder, ir manā priekšā. Tie tūkstoš sudraba gabali ir priekš tevis, Salaman! Bet divsimt ir priekš viņa augļu sargiem.
13 Iwe amene umakhala mʼminda uli pamodzi ndi anzako, ndilole kuti ndimve liwu lako!
Tu, kas tais dārzos dzīvo, tie biedri tavu balsi ņem vērā, dodi man to dzirdēt.
14 Fulumira wokondedwa wanga, ndipo ukhale ngati gwape kapena mwana wa mbawala wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.
Steidzies, mans draugs, un esi tā kā stirna vai kā jauns briedis pa smaržīgiem puķu kalniem.

< Nyimbo ya Solomoni 8 >