< Nyimbo ya Solomoni 8 >

1 Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga, amene anayamwa mawere a amayi anga! Ndikanakumana nawe pa njira, ndikanakupsompsona, ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.
O that thou wert as my brother, That sucked the breast of my mother! When I found thee abroad, I might kiss thee; And for it no one would deride me.
2 Ndikanakutenga ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, amayi amene anandiphunzitsa, ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe, zotsekemera za makangadza.
I will lead thee, and bring thee into my mother's house, that thou mayst teach me; I will give thee spiced wine to drink, and the juice of my pomegranates.
3 Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.
His left hand is under my head, And his right hand embraceth me.
4 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani: musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
[[Lov.]] I charge you, O ye daughters of Jerusalem! That ye stir not up, nor awake my love, Till she please!
5 Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo, atatsamira wokondedwa wakeyo? Mkazi Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi, pamenepo ndi pamene amayi anachirira, pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.
[[Lad.]] Who is this that cometh up from the wilderness, Leaning upon her beloved? [[M.]] Under the apple-tree I awakened thee; There thy mother brought thee forth; There she that bore thee brought thee forth!
6 Undiyike pamtima pako ngati chidindo, ngati chidindo cha pa dzanja lako; pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa, nsanje ndiyaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti lawilawi ngati malawi a moto wamphamvu. (Sheol h7585)
O set me as a seal upon thy heart, As a seal upon thine arm! For love is strong as death; True love is firm as the grave: Its flames are flames of fire, The fire of Jehovah. (Sheol h7585)
7 Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi, mitsinje singachikokolole chikondicho. Ngati wina apereka chuma chonse cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi, adzangonyozeka nazo kotheratu.
Many waters cannot quench love, Nor can floods drown it. Would a man give all the wealth of his house for love, It would be utterly contemned.
8 Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono, koma alibe mawere, kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu pa tsiku limene adzamufunsire?
[[Br.]] We have a sister who is yet young; She is yet without breasts. What shall we do with our sister, When she shall be spoken for?
9 Ngati iye ndi khoma, tidzamumangira nsanja ya siliva. Ngati iye ndi chitseko, tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.
If she be a wall, We will build upon it a silver tower; If she be an open gate, We will inclose her with planks of cedar.
10 Ine ndili ngati khoma, ndipo mawere anga ndi nsanja zake. Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa ndine wobweretsa mtendere.
[[Sis.]] I am a wall, and my breasts like towers; Therefore am I become in his eyes as one that findeth peace.
11 Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni; iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi, aliyense mwa iwo ankayenera kupereka ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.
Solomon had a vineyard at Baal-hamon; He let out the vineyard to keepers; Every one was to bring a thousand shekels of silver for its fruit.
12 Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha. Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000 ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.
My vineyard is before my eyes. Be thine the thousand, O Solomon! And two hundred to the keepers of its fruit!
13 Iwe amene umakhala mʼminda uli pamodzi ndi anzako, ndilole kuti ndimve liwu lako!
[[Lov.]] Thou that dwellest in the gardens! Friends listen to thy voice; Let me hear thee!
14 Fulumira wokondedwa wanga, ndipo ukhale ngati gwape kapena mwana wa mbawala wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.
Fly, my beloved! like a gazelle, or a young hind, Upon the mountains of spices.

< Nyimbo ya Solomoni 8 >