< Nyimbo ya Solomoni 7 >
1 Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
"Huru sköna äro icke dina fötter i sina skor, du ädla! Dina höfters rundning är såsom ett bröstspännes kupor, gjorda av en konstnärs händer.
2 Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
Ditt sköte är en rundad skål, må vinet aldrig fattas däri. Din midja är en vetehög, omhägnad av liljor.
3 Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
Din barm är lik ett killingpar, tvillingar av en gasell.
4 Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
Din hals liknar Elfenbenstornet, dina ögon dammarna i Hesbon, vid Bat-Rabbimsporten. Din näsa är såsom Libanonstornet, som skådar ut mot Damaskus.
5 Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
Ditt huvud höjer sig såsom Karmel, och lockarna på ditt huvud hava purpurglans. En konung är fångad i deras snara." ----
6 Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
"Huru skön och huru ljuv är du icke, du kärlek, så följd av lust!
7 Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
Ja, din växt är såsom ett palmträds, och din barm liknar fruktklasar.
8 Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
Jag tänker: I det palmträdet vill jag stiga upp, jag vill gripa tag i dess kvistar. Må din barm då vara mig såsom vinträdets klasar och doften av din andedräkt såsom äpplens doft
9 ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
och din mun såsom ljuvaste vin!" "Ja, ett vin som lätt glider ned i min vän och fuktar de slumrandes läppar.
10 Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
Jag är min väns, och till mig står hans åtrå." ----
11 Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
Kom, min vän; låt oss gå ut på landsbygden och stanna i byarna över natten.
12 Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
Bittida må vi gå till vingårdarna, för att se om vinträden hava slagit ut, om knopparna hava öppnat sig, om granatträden hava fått blommor. Där vill jag giva min kärlek åt dig.
13 Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.
Kärleksäpplena sprida sin doft, och vid våra dörrar finnas alla slags ädla frukter, både nya och gamla; åt dig, min vän, har jag förvarat dem.