< Nyimbo ya Solomoni 7 >

1 Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
Cât de minunate sunt picioarele tale cu sandale, fiică de prinţ! Rotunjimile coapselor tale sunt ca bijuterii, lucrarea mâinilor unui meşteşugar iscusit.
2 Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
Buricul tău este ca o cupă rotundă, căruia nu îi lipseşte licoarea; pântecele tău o movilă de grâu înconjurată cu crini.
3 Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
Cei doi sâni ai tăi sunt ca două căprioare tinere ce sunt gemene.
4 Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
Gâtul tău este ca un turn de fildeş; ochii tăi precum iazurile în Hesbon, de lângă poarta Batrabimului; nasul tău este ca turnul Libanului care priveşte spre Damasc.
5 Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
Capul tău, peste tine, este precum Carmelul, şi părul capului tău ca purpura; împăratul este ţinut în galeriile tale.
6 Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
Cât de frumoasă şi cât de plăcută eşti tu, iubirea mea, pentru desfătări!
7 Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
Această statură a ta este ca un palmier şi sânii tăi ca ciorchini de struguri.
8 Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
Am spus: Mă voi urca în palmier, îi voi apuca crengile; acum de asemenea sânii tăi vor fi ca ciorchinii viţei şi mirosul feţei tale ca mere;
9 ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
Şi cerul gurii tale, pentru preaiubitul meu, ca cel mai bun vin care curge cu dulceaţă, făcând buzele celor adormiţi să vorbească.
10 Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
Eu sunt a preaiubitului meu şi dorinţa lui este spre mine.
11 Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
Vino, preaiubitul meu, să mergem în câmp; să găzduim în sate.
12 Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
Să ne urcăm devreme la vii; să vedem dacă viţa înfloreşte, dacă floarea strugurilor se arată şi dacă rodiile înmuguresc; acolo îţi voi da iubirile mele.
13 Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.
Mandragorele răspândesc miros şi la porţile noastre sunt tot felul de fructe plăcute, noi şi vechi, pe care le-am păstrat pentru tine, preaiubitul meu.

< Nyimbo ya Solomoni 7 >