< Nyimbo ya Solomoni 7 >

1 Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
Hvor skønne ere dine Trin i Skoene, du ædelbaarne! dine Lænders Bøjninger ere som Smykker, Værk af Kunstnerhaand.
2 Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
Din Navle er det runde Bæger, — det mangler aldrig krydret Vin, din Bug er en Hvededynge, omhegnet med Lillier.
3 Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
Dine to Bryster ere ligesom to unge Raatvillinger.
4 Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
Din Hals er som Elfenbenstaarnet, dine Øjne ere Fiskedamme i Hesbon ved Bath-Rabbins Port, din Næse er som Libanons Taarn, der skuer ud imod Damaskus.
5 Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
Dit Hoved paa dig er som Karmel, og Haaret paa dit Hoved er som Purpur; Kongen er fængslet i Lokkerne.
6 Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
Hvor dejlig og hvor yndig er du, o kære! i Elskelighed.
7 Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
Denne din ranke Vækst er ligt et Palmetræ og dine Bryster som Drueklaser.
8 Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
Jeg sagde: Jeg vil stige op i Palmetræet, jeg vil tage fat paa dets Grene; og dine Bryster vorde som Vinstokkens Drueklaser og din Næses Aande som Æblerne;
9 ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
og din Gane som den gode Vin, der gaar glat ned for min elskede og bringer sovendes Læber til at tale.
10 Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
Jeg er min elskedes, og til mig er hans Attraa.
11 Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
Kom, min elskede! lader os gaa ud paa Marken, lader os blive Natten over i Landsbyerne!
12 Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
Lader os aarle gaa til Vingaardene, lader os se, om Vinstokken har skudt, om Blomsterne ere udsprungne, og om Granattræerne blomstre; der vil jeg skænke dig min Kærlighed.
13 Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.
Dudaim give Lugt, og ved vore Døre er der alle Haande kostelige Frugter, nye og gamle; o, min elskede! jeg har gemt dem til dig.

< Nyimbo ya Solomoni 7 >