< Nyimbo ya Solomoni 7 >

1 Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
Kako su krasni koraci tvoji u sandalama, kćeri kneževska! Pregibi su bokova tvojih kao grivne stvorene rukom umjetnika.
2 Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
Pupak ti je kao okrugla čaša koja nikad nije bez pića. Trbuh ti je kao stog pšenice ograđen ljiljanima.
3 Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
Dvije su dojke tvoje dva laneta, blizanca košutina.
4 Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
Vrat je tvoj kao kula bjelokosna. Oči su tvoje kao ribnjaci u Hešbonu kod vrata batrabimskih. Nos ti je kao kula libanska što gleda prema Damasku.
5 Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
Glava je tvoja kao brdo Karmel, a kosa na glavi kao purpur i kralj se zapleo u njene pletenice.
6 Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
Kako si lijepa i kako si ljupka, o najdraža, među milinama!
7 Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
Stas je tvoj kao palma, grudi su tvoje grozdovi.
8 Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
Rekoh: popet ću se na palmu da dohvatim vrške njezine, a grudi će tvoje biti kao grozdovi na lozi, miris daha tvoga kao jabuke.
9 ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
Usta su tvoja kao najbolje vino. Koje odlazi ravno dragome mome kao što teče na usnama usnulih.
10 Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
Ja pripadam dragome svome i on je željan mene.
11 Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
Dođi, dragi moj, ići ćemo u polja, noćivat ćemo u selima.
12 Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
Jutrom ćemo ići u vinograde da vidimo pupa li loza, zameće li se grožđe, jesu li procvali mogranji. Tamo ću ti dati ljubav svoju.
13 Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.
Mandragore šire miris, u našim kućama ima svakog voća, novoga i starog, za te sam ga čuvala, o najdraži moj!

< Nyimbo ya Solomoni 7 >