< Nyimbo ya Solomoni 6 >

1 Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti? Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?
[[Lad.]] Whither is thy beloved gone, thou fairest among women? Whither hath thy beloved betaken himself? That we may seek him with thee.
2 Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake, ku timinda ta zokometsera zakudya, akukadyetsa ziweto zake ku minda, ndiponso akuthyola maluwa okongola.
[[M.]] My beloved is gone down to his garden, To the beds of balsam, To feed in the gardens, And to gather lilies.
3 Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga; amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.
I am my beloved's, and my beloved is mine; He feedeth among the lilies.
4 Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza, wokongola kwambiri ngati Yerusalemu, ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.
Beautiful art thou, my love, as Tirzah, Lovely as Jerusalem; But terrible as an army with banners.
5 Usandipenyetsetse; pakuti maso ako amanditenga mtima. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
Turn away thine eyes from me! They overpower me! Thy locks are like a flock of goats, Which lie down upon Gilead.
6 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa, iliyonse ili ndi ana amapasa, palibe imene ili yokha.
Thy teeth are like a flock of sheep, Which come up from the washing-place, Of which every one hath twins, And none is barren among them.
7 Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu, masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.
As a divided pomegranate Are thy cheeks behind thy veil.
8 Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60, ndi azikazi 80, ndi anamwali osawerengeka;
Threescore are the queens, and fourscore the concubines, And the maidens without number.
9 koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense; mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake, mwana wapamtima wa amene anamubereka. Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala; akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.
But my dove, my undefiled, is the one; She is the incomparable one of her mother, The darling of her that bore her. The daughters saw her, and blessed her; The queens and concubines, and they praised her.
10 Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha, wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa, wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?
[[Lov.]] Who is this that looketh forth like the morning, Fair as the moon, bright as the sun, And terrible as an army with banners?
11 Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa, kukaona ngati mpesa waphukira kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.
[[M.]] I went down into the garden of nuts, To see the green plants of the valley, To see whether the vine blossomed, And the pomegranates budded.
12 Ndisanazindikire kanthu, ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.
Or ever I was aware, My soul had made me like the chariots of the prince's train.
13 Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami; bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe! Mwamuna Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami, pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?
[[Lad.]] Return, return, O Shulamite! Return, return, that we may look upon thee! [[M.]] Why should ye look upon the Shulamite, As upon a dance of the hosts?

< Nyimbo ya Solomoni 6 >