< Nyimbo ya Solomoni 5 >

1 Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
Дођох у врт свој, сестро моја невесто, берем смирну своју и мирисе своје, једем саће своје и мед свој, пијем вино своје и млеко своје; једите, пријатељи, пијте, и опијте се, мили моји!
2 Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
Ја спавам, а срце је моје будно; ето гласа драгог мог, који куца: Отвори ми, сестро моја, драга моја, голубице моја, безазлена моја; јер је глава моја пуна росе и коса моја ноћних капи.
3 Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
Свукла сам хаљину своју, како ћу је обући? Опрала сам ноге своје, како ћу их каљати?
4 Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
Драги мој промоли руку своју кроз рупу, а шта је у мени устрепта од њега.
5 Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
Ја устах да отворим драгом свом, а с руку мојих прокапа смирна, и низ прсте моје потече смирна на држак од браве.
6 Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
Отворих драгом свом, али драгог мог не беше, отиде. Бејах изван себе кад он проговори. Тражих га, али га не нађох; виках га, али ми се не одазва.
7 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
Нађоше ме стражари, који обилазе по граду, бише ме, ранише ме, узеше превес мој с мене стражари по зидовима.
8 Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
Заклињем вас, кћери јерусалимске, ако нађете драгог мог, шта ћете му казати? Да сам болна од љубави.
9 Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
Шта је твој драги бољи од других драгих, о најлепша међу женама? Шта је твој драги бољи од других драгих, те нас тако заклињеш?
10 Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
Драги је мој бео и румен, заставник између десет хиљада;
11 Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
Глава му је најбоље злато, коса му је кудрава, црна као гавран;
12 Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
Очи су му као у голуба на потоцима воденим, млеком умивене, и стоје у обиљу;
13 Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
Образи су му као лехе мирисног биља, као цвеће мирисно; усне су му као љиљан, с њих капље смирна житка;
14 Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
На рукама су му златни прстени, на којима су уковани вирили; трбух му је као светла слонова кост обложена сафирима.
15 Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
Гњати су му као ступови од мрамора, углављени на златном подножју; стас му је Ливан, красан као кедри.
16 Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.
Уста су му слатка и сав је љубак. Такав је мој драги, такав је мој мили, кћери јерусалимске.

< Nyimbo ya Solomoni 5 >