< Nyimbo ya Solomoni 5 >
1 Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
[[Lov.]] I am come to my garden, my sister, my spouse! I gather my myrrh with my balsam, I eat my honeycomb with my honey, I drink my wine with my milk. Eat, O friends! Drink, yea, drink abundantly, my loved companions!
2 Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
[[M.]] I slept, but my heart was awake; It was the voice of my beloved, who was knocking: “Open to me, my sister, my love, My dove, my perfect one! For my head is filled with dew, And my locks with the drops of the night.”
3 Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
“I have taken off my vest [[said I]]; How shall I put it on? I have washed my feet; How shall I soil them?”
4 Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
My beloved put in his hand by the hole of the door, And my heart was moved for him.
5 Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
I rose up to open to my beloved, And my hands dropped with myrrh, And my fingers with self-flowing myrrh, upon the handles of the bolt.
6 Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
I opened to my beloved; But my beloved had withdrawn himself, and was gone. I was not in my senses while he spake with me! I sought him, but could not find him; I called him, but he gave me no answer.
7 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
The watchmen that go about the city found me; They smote me, they wounded me; The keepers of the walls took away from me my veil.
8 Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
I charge you, O ye daughters of Jerusalem! If ye should find my beloved, —What will ye tell him? That I am sick with love.
9 Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
[[Lad.]] What is thy beloved more than another beloved, O thou fairest among women! What is thy beloved more than another beloved, That thus thou dost charge us?
10 Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
[[M.]] My beloved is white and ruddy, The chief among ten thousand.
11 Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
His head is as the most fine gold; His locks waving palm-branches, Black as a raven;
12 Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
His eyes are doves by streams of water, Washed with milk, dwelling in fulness;
13 Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
His cheeks are like a bed of balsam, Like beds of spices; His lips are lilies Dropping self-flowing myrrh;
14 Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
His hands are gold rings set with chrysolite; His body is wrought-work of ivory, overlaid with sapphires;
15 Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
His legs are marble pillars, resting on pedestals of fine gold; His aspect is like Lebanon, Majestic like the cedars;
16 Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.
His mouth is sweetness; His whole being, loveliness. This is my beloved, This my friend, O ye daughters of Jerusalem!