< Nyimbo ya Solomoni 4 >
1 Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga! Ndithudi, ndiwe wokongola! Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
Лепа ти си, драга моја, лепа ти си, очи су ти као у голубице између витица твојих; коса ти је као стадо коза које се виде на гори Галаду;
2 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene, zochokera kozisambitsa kumene. Iliyonse ili ndi ana amapasa; palibe imene ili yokha.
Зуби су ти као стадо оваца једнаких, кад излазе из купала, које се све близне, а ниједне нема јалове.
3 Milomo yako ili ngati mbota yofiira; pakamwa pako ndi pokongola kwambiri. Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
Усне су ти као конац скерлета, а говор ти је љубак; као кришка шипка јагодице су твоје између витица твојих;
4 Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide, yomangidwa bwino ndi yosalala; pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000, zishango zonsezo za anthu ankhondo.
Врат ти је као кула Давидова сазидана за оружје, где висе хиљадама штитови и свакојако оружје јуначко;
5 Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala, ngati ana amapasa a nswala amene akudya pakati pa maluwa okongola.
Две су ти дојке као два ланета близанца, који пасу међу љиљанима.
6 Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira ndipo mithunzi ikayamba kuthawa, ndidzapita ku phiri la mure ndi ku chitunda cha lubani.
Док дан захлади и сенке отиду, ићи ћу ка гори смирновој и ка хуму тамјановом.
7 Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga; palibe chilema pa iwe.
Сва си лепа драга моја, и нема недостатака на теби.
8 Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga, tiye tichoke ku Lebanoni, utsikepo pa msonga ya Amana, kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni, kuchoka ku mapanga a mikango ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
Ходи са мном с Ливана, невесто, ходи са мном с Ливана, да гледаш с врха аманског, с врха сенирског и ермонског, из пећина лавовских, с гора рисовских.
9 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima, iwe wanditenga mtima ndi kapenyedwe ka maso ako, ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
Отела си ми срце, сестро моја невесто, отела си ми срце једним оком својим и једним ланчићем с грла свог.
10 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa! Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo, ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
Лепа ли је љубав твоја, сестро моја невесто, боља је од вина љубав твоја, и мирис уља твојих од свих мирисних ствари.
11 Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi; pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi. Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
С усана твојих капље саће, невесто, под језиком ти је мед и млеко, и мирис је хаљина твојих као мирис ливански.
12 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa; ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
Ти си као врт затворен, сестро моја невесто, извор затворен, студенац запечаћен.
13 Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza; muli zipatso zokoma kwambiri, muli hena ndi nadi,
Биље је твоје воћњак од шипака с воћем красним, од кипра и нарда.
14 nadi ndi safiro, kalamusi ndi sinamoni, komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino. Mulinso mure ndi aloe ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
Од нарда и шафрана, од иђирота и цимета са свакојаким дрвљем за кад, од смирне и алоја и са сваким прекрасним мирисима.
15 Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda, chitsime cha madzi oyenda, mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.
Изворе вртовима, студенче воде живе и која тече с Ливана!
16 Dzuka, iwe mphepo yakumpoto, ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera! Uzira pa munda wanga, kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse. Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.
Устани севере, и ходи јуже, и дуни по врту мом да капљу мириси његови; нека дође драги мој у врт свој, и једе красно воће своје.