< Nyimbo ya Solomoni 4 >

1 Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga! Ndithudi, ndiwe wokongola! Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
Khangela, umuhle, mthandwa wami, khangela, umuhle. Amehlo akho angawamajuba ngaphakathi kweveyili lakho; inwele zakho zinjengomhlambi wembuzi zisehla entabeni iGileyadi.
2 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene, zochokera kozisambitsa kumene. Iliyonse ili ndi ana amapasa; palibe imene ili yokha.
Amazinyo akho anjengomhlambi wezimvukazi ezigundiweyo, ezikhuphuka ekugezisweni, okuthi zonke zazo zizele amaphahla, njalo kungekho efelwayo phakathi kwazo.
3 Milomo yako ili ngati mbota yofiira; pakamwa pako ndi pokongola kwambiri. Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
Indebe zakho zinjengentambo ebomvu, lenkulumo yakho yinhle. Inhlafuno zakho phakathi kweveyili lakho zinjengocezu lwepomegranati.
4 Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide, yomangidwa bwino ndi yosalala; pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000, zishango zonsezo za anthu ankhondo.
Intamo yakho injengomphotshongo kaDavida owakhiwe waba yindlu yezikhali, okulenga kuwo amahawu ayinkulungwane, wonke ayizihlangu zamaqhawe.
5 Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala, ngati ana amapasa a nswala amene akudya pakati pa maluwa okongola.
Amabele akho womabili anjengabantwana ababili bomziki, abangamaphahla empala, abadla phakathi kwemiduze.
6 Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira ndipo mithunzi ikayamba kuthawa, ndidzapita ku phiri la mure ndi ku chitunda cha lubani.
Kuze kube semadabukakusa, lamathunzi abaleke, mina ngizakuya entabeni yemure, leqaqeni lwempepha.
7 Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga; palibe chilema pa iwe.
Wena wonke umuhle, mthandwa wami, kakukho sici kuwe.
8 Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga, tiye tichoke ku Lebanoni, utsikepo pa msonga ya Amana, kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni, kuchoka ku mapanga a mikango ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
Woza lami sisuke eLebhanoni, makoti wami, lami sisuke eLebhanoni. Khangela usengqongeni yeAmana, engqongeni yeSeniri leyeHermoni, ezimbalwini zezilwane, entabeni zezingwe.
9 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima, iwe wanditenga mtima ndi kapenyedwe ka maso ako, ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
Uyithumbile inhliziyo yami, dadewethu, makoti, uyithumbile inhliziyo yami ngelinye lamehlo akho, ngesigqizo esisodwa sentamo yakho.
10 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa! Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo, ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
Luhle kangakanani uthando lwakho, dadewethu, makoti! Lungcono kangakanani uthando lwakho kulewayini, lephunga lamagcobo akho kulamakha wonke.
11 Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi; pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi. Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
Indebe zakho, makoti, zithonta njengohlanga loluju; uluju lochago kungaphansi kolimi lwakho, lephunga lezembatho zakho linjengephunga leLebhanoni.
12 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa; ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
Uyisivande esikhiyiweyo, dadewethu, makoti, umthombo okhiyiweyo, isiphethu esinanyekwe ngophawu.
13 Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza; muli zipatso zokoma kwambiri, muli hena ndi nadi,
Amahlumela akho ayisivande samapomegranati, lezithelo ezimnandi, ihena lenadi,
14 nadi ndi safiro, kalamusi ndi sinamoni, komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino. Mulinso mure ndi aloe ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
inadi lesafroni, ikhalamu lekinamoni, lezihlahla zonke zempepha, imure lenhlaba, lamakha wonke aqakathekileyo;
15 Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda, chitsime cha madzi oyenda, mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.
umthombo wezivande, umgodi wamanzi aphilayo, lezifula ezivela eLebhanoni.
16 Dzuka, iwe mphepo yakumpoto, ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera! Uzira pa munda wanga, kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse. Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.
Vuka, moya wenyakatho, uze lawe, moya weningizimu, uphephethe esivandeni sami ukuze amakha aso ageleze aphume. Kasize isithandwa sami esivandeni saso, sidle izithelo zaso ezimnandi.

< Nyimbo ya Solomoni 4 >