< Nyimbo ya Solomoni 4 >
1 Ndiwe wokongoladi wokondedwa wanga! Ndithudi, ndiwe wokongola! Maso ako ali ngati nkhunda kumbuyo kwa nsalu yophimba kumutu. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
Hvor du er fager, min veninde, hvor er du fager! Dine Øjne er Duer bag sløret, dit Hår som en Gedeflok bølgende ned fra Gilead,
2 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zomwe zangometedwa kumene, zochokera kozisambitsa kumene. Iliyonse ili ndi ana amapasa; palibe imene ili yokha.
dine Tænder som en nyklippet Fåreflok, der kommer fra Bad, som alle har Tvillinger, intet er uden Lam;
3 Milomo yako ili ngati mbota yofiira; pakamwa pako ndi pokongola kwambiri. Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutuyo, masaya ako akuoneka ngati mabandu a makangadza.
som en Purpursnor er dine Læber, yndig din Mund, din Tinding som et bristet Granatæble bag ved dit Slør;
4 Khosi lako lili ngati nsanja ya Davide, yomangidwa bwino ndi yosalala; pa nsanja imeneyo pali zishango 1,000, zishango zonsezo za anthu ankhondo.
din Hals er som Davids Tårn, der er bygget til Udkig, tusinde Skjolde hænger derpå, kun Helteskjolde;
5 Mawere ako ali ngati tiana tiwiri ta nswala, ngati ana amapasa a nswala amene akudya pakati pa maluwa okongola.
dit Bryst som to Hjortekalve, Gazelle tvillinger, der græsser blandt Liljer.
6 Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira ndipo mithunzi ikayamba kuthawa, ndidzapita ku phiri la mure ndi ku chitunda cha lubani.
Til Dagen svales og Skyggerne længes, vil jeg vandre til Myrrabjerget og Vellugtshøjen.
7 Ndiwe wokongola kwambiri wokondedwa wanga; palibe chilema pa iwe.
Du er fuldendt fager, min Veninde og uden Lyde.
8 Tiye tichoke ku Lebanoni iwe mkwatibwi wanga, tiye tichoke ku Lebanoni, utsikepo pa msonga ya Amana, kuchoka pa msonga ya phiri la Seniri, pamwamba penipeni pa Herimoni, kuchoka ku mapanga a mikango ndiponso kumapiri kumene akambuku amavutitsa.
Kom med mig fra Libanon, Brud, kom med mig fra Libanon, stig ned fra Amanas Tinde, fra Senirs og Hermons Tinde, fra Løvers Huler, fra Panteres Bjerge!
9 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, wanditenga mtima, iwe wanditenga mtima ndi kapenyedwe ka maso ako, ndiponso ndi umodzi mwa mikanda ya mʼkhosi mwako.
Du har fanget mig, min Søster, min Brud, du har fanget mig med et af dine Blikke, med en af din Halses Kæder.
10 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, chikondi chako nʼchosangalatsa! Chikondi chako nʼchosangalatsa kwambiri kupambana vinyo, ndiponso fungo la mafuta ako ndi lopambana zonunkhiritsa zonse!
Hvor herlig er din Kærlighed, min Søster, min Brud, hvor din Kærlighed er god fremfor Vin, dine Salvers Duft fremfor alskens Vellugt!
11 Iwe mkwatibwi wanga, milomo yako ikuchucha uchi ngati chisa cha njuchi; pansi pa lilime lako pali mkaka ndi uchi. Fungo lonunkhira la zovala zako likumveka ngati fungo la ku Lebanoni.
Dine Læber drypper af Sødme, min Brud, under din Tunge er Honning og Mælk; dine Klæders Duft er som Libanons Duft.
12 Iwe mlongo wanga, mkwatibwi wanga, ndiwe munda wopiringidzidwa; ndiwe kasupe wotchingidwa, chitsime chotetezedwa.
Min Søster, min Brud er en lukket Have, en lukket Kilde, et Væld under Segl.
13 Zomera zako ndi munda wa zipatso za makangadza; muli zipatso zokoma kwambiri, muli hena ndi nadi,
Dine Skud er en Lund af Granattræer med kostelige Frugter, Kofer,
14 nadi ndi safiro, kalamusi ndi sinamoni, komanso mtengo uliwonse wonunkhira bwino. Mulinso mure ndi aloe ndi zonunkhiritsa zonse zabwino kwambiri.
Nardus og Kalmus og Kanel og alle Slags Vellugtstræer, Myrra og Safran og Aloe og alskens ypperlig Balsam.
15 Iwe ndiwe kasupe wa mʼmunda, chitsime cha madzi oyenda, mtsinje wa madzi ochokera ku Lebanoni.
Min Haves Væld er en Brønd med rindende Vand og Strømme fra Libanon.
16 Dzuka, iwe mphepo yakumpoto, ndipo bwera, iwe mphepo yakummwera! Uzira pa munda wanga, kuti fungo lake lonunkhira lifalikire ponseponse. Bwenzi langa alowe mʼmunda mwake ndi kudya zipatso zake zabwino kwambiri.
Nordenvind, vågn, Søndenvind kom, blæs gennem min Have, så dens Vellugt spredes! Min Ven komme ind i sin Have og nyde dens udsøgte Frugt!