< Nyimbo ya Solomoni 2 >
1 Ine ndine duwa la ku Saroni, duwa lokongola la ku zigwa.
Es esmu roze Šaronā un lilija ielejā.
2 Monga duwa lokongola pakati pa minga ndi momwe alili wokondedwa wanga pakati pa atsikana.
Tā kā lilija starp ērkšķiem, tāda ir mana draudzene starp tām meitām.
3 Monga mtengo wa apulosi pakati pa mitengo ya mʼnkhalango ndi momwe alili bwenzi langa pakati pa anyamata. Ndimakondwera kukhala pansi pa mthunzi wako, ndipo chipatso chake ndi chokoma mʼkamwa mwanga.
Tā kā ābele starp meža kokiem, tāds ir mans draugs starp tiem dēliem. Es ilgojos sēdēt viņa pavēnī, un viņa auglis manai mutei salds.
4 Iye wanditengera ku nyumba yaphwando, ndipo mbendera yake yozika pa ine ndi chikondi.
Viņš mani ved vīna namā, un mīlestība ir viņa karogs pār mani.
5 Undidyetse keke ya mphesa zowuma, unditsitsimutse ndi ma apulosi, pakuti chikondi chandifowoketsa.
Atspirdzinājiet mani ar vīna ogām un spēcinājiet mani ar āboliem; jo es nīkstu no mīlestības.
6 Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere, ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.
Viņa kreisā roka ir apakš manas galvas, un viņa labā roka mani apkampj.
7 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo: Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
Es jūs mīļi lūdzu, jūs Jeruzālemes meitas, pie tām stirnām un kalnu kazām laukā, neuztraucat un nemodinājat mīlestību, kamēr tai pašai patīk.
8 Tamverani bwenzi langa! Taonani! Uyu akubwera apayu, akulumphalumpha pa mapiri, akujowajowa pa zitunda.
Šī ir mana drauga balss; redzi, viņš nāk un lēkā pa tiem kalniem un deij pa tiem pakalniem.
9 Bwenzi langa ali ngati gwape kapena mwana wa mbawala. Taonani! Uyo wayima kuseri kwa khoma lathulo, akusuzumira mʼmazenera, akuyangʼana pa mpata wa zenera.
Mans draugs ir līdzīgs stirnai vai jaunam briedim. Redzi, viņš stāv aiz sienas, skatās caur logiem un raugās caur skadriņiem.
10 Bwenzi langa anayankha ndipo anati kwa ine, “Dzuka bwenzi langa, wokongola wanga, ndipo tiye tizipita.
Mans draugs atbild un saka uz mani: celies, mana draudzene, mana skaistā, un nāc!
11 Ona, nyengo yozizira yatha; mvula yatha ndipo yapitiratu.
Jo redzi, ziema ir pagājusi, stiprais lietus jau ir pārgājis un nost.
12 Maluwa ayamba kuoneka pa dziko lapansi; nthawi yoyimba yafika, kulira kwa njiwa kukumveka mʼdziko lathu.
Puķes rādās laukā, dziesmu laiks atnācis, un ūbeles balss dzirdama mūsu zemē.
13 Mtengo wankhuyu ukubereka zipatso zake zoyambirira; mitengo ya mpesa ya maluwa ikutulutsa fungo lake. Dzuka bwenzi langa, wokongola wanga tiye tizipita.”
Vīģes koks dabūjis pumpurus, un vīna koki plaukst un dod smaržu; celies, nāc, mana draudzene, mana skaistā, nāc šurp!
14 Nkhunda yanga yokhala mʼmingʼalu ya thanthwe, mʼmalo obisala a mʼmbali mwa phiri, onetsa nkhope yako, nʼtamvako liwu lako; pakuti liwu lako ndi lokoma, ndipo nkhope yako ndi yokongola.
Mans balodis akmeņu kalnos, apslēptos plaisumos, parādi man savu vaigu, dod man savu balsi dzirdēt; jo tava balss ir salda, un tavs vaigs ir mīlīgs.
15 Mutigwirire nkhandwe, nkhandwe zingʼonozingʼono zimene zikuwononga minda ya mpesa, minda yathu ya mpesa imene yayamba maluwa.
Gūstat mums lapsas, tās mazās lapsas, kas vīna dārzus maitā, jo mūsu vīna dārzi stāv ziedos.
16 Bwenzi langa ndi wangadi ndipo ine ndine wake; amadyetsa gulu lake la ziweto pakati pa maluwa okongola.
Mans draugs ir mans, es esmu viņa, kas pa tām lilijām gana.
17 Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira ndipo mithunzi ikayamba kuthawa, unyamuke bwenzi langa, ndipo ukhale ngati gwape kapena ngati mwana wa mbawala pakati pa mapiri azigwembezigwembe.
Kamēr diena metās dzestra un ēnas bēg, atgriezies, mans draugs, kā stirna, vai kā jauns briedis pa kalnu plaisumiem.