< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
Ingoma yezingoma kaSolomoni.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Kangange ngezangiwo zomlomo wakhe ngoba uthando lwakho lumnandi kulewayini.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Limnandi iphunga lamagcobo akho; ibizo lakho linjengamakha atheliweyo. Yikho izintombi zikuthanda kangaka!
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Ngithatha uhambe lami, kasiphangise! Inkosi kayingingenise endlini yayo. Abangane Siyathokoza njalo siyajabula ngawe; sizalubabaza uthando lwakho okudlula iwayini. Umlobokazi Kabazenzi ukuba bakuthande!
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Ngimnyama kodwa ngiyabukeka, lina madodakazi aseJerusalema ngimnyama okwamathente aseKhedari, okwamakhetheni amathente kaSolomoni.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Linganginyonkolozi ngoba ngimnyama, ngimnyama ngenxa yokutshiswa lilanga. Abanewethu bangizondela bangenza umlindi wesivini; angabe ngisanaka esami isivini.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Akungitshele, wena engikuthandayo, uyelusela ngaphi imihlambi yezimvu zakho lokuthi ziphumula ngaphi izimvu zakho emini? Kungani ngisiba njengomfazi ombozileyo eceleni kwemihlambi yabangane bakho na?
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
Nxa ungazi, wena omuhle okudlula bonke abesifazane, landela umkhondo wezimvu udlisele amazinyane embuzi zakho eduze lamathente abelusi.
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
Sithandwa sami, ngikufanisa lebhiza elisikazi elibotshwe enqoleni kaFaro.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Izihlathi zakho zinhle ngokuceciswa, intamo yakho ngobuhlalu obucazimulayo.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Sizakwenzela amacici egolide, ebalazwe ngesiliva.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
Khonapho inkosi isetafuleni amakha ami enadi alanquza iphunga lawo elimnandi.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
Kimi isithandwa sami sinjengemfuko yemure ithe khoxo phakathi kwamabele ami.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
Kimi isithandwa sami sinjengelixha lempoko zehena eliphuma esivinini se-Eni-Gedi.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
Bakithi, umuhle njani sithandwa sami! Ngeqiniso umuhle! Amehlo akho angamajuba.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Umuhle ngempela, sithandwa sami! Bakithi, uyabukeka! Umbheda wethu butshani obuluhlaza tshoko.
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
Izinsika zendlu yethu ngezomsedari lezintungo ngezefire.

< Nyimbo ya Solomoni 1 >