< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
Énekek éneke, Salamontól.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Csókoljon engem szája csókjaival: mert bornál jobb a szerelmed.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Illatnak jók az olajaid, kiöntött olaj a neved; azért szeretnek téged a leányzók.
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Vonj engem, utánad hadd szaladjunk – termeibe bevitt engem a király – hadd ujjongjunk és örvendjünk benned, hadd emlegessük szerelmedet inkább a bornál: méltán szeretnek téged.
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Fekete vagyok, de szép, ti Jeruzsálem leányai, mint Kédár sátrai, mint Salamon szőnyegei.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Ne nézzetek rám, hogy kissé fekete vagyok, hogy lesütött engem a nap! Anyám fiai megharagudtak reám, tettek engem őrzőjévé a szőlőknek: a magam szőlőjét nem őriztem.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Mondd meg nekem te, kit lelkem szeret, merre legeltetsz, merre heverésztetsz délben? Mert minek legyek, mint aki elburkolja magát, társaid nyájainál?
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
Ha te ezt nem tudod, legszebbike az asszonyoknak, indulj el a juhok nyomdokain és legeltesd gödölyéidet a pásztorok hajlékainál.
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
Paripámhoz Fáraó szekereinél mondlak hasonlónak, kedvesem!
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Bájosak az orczáid a füzérekben, nyakad a gyöngysorokban.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Aranyfüzéreket készítünk neked ezüst gombocskákkal.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
Mialatt a király asztalkörében ült, az én nárdusom megadta illatát.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
Myrrhacsokor az én barátom nekem, mely kebleim között piben;
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
cziprusfürt az én barátom nekem, Én-Gédi szőlőiben.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
Íme, szép vagy te kedvesem, íme, szép vagy, szemeid galambok.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Íme, szép vagy te barátom, kedves is, nyoszolyánk is zöldelő;
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
házaink gerendái czédrusok, padozatunk cziprusok.

< Nyimbo ya Solomoni 1 >