< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
The Song of Songs, that [is] Solomon's.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Let him kiss me with kisses of his mouth, For better [are] thy loves than wine.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
For fragrance [are] thy perfumes good. Perfume emptied out — thy name, Therefore have virgins loved thee!
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Draw me: after thee we run, The king hath brought me into his inner chambers, We do joy and rejoice in thee, We mention thy loves more than wine, Uprightly they have loved thee!
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Dark [am] I, and comely, daughters of Jerusalem, As tents of Kedar, as curtains of Solomon.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Fear me not, because I [am] very dark, Because the sun hath scorched me, The sons of my mother were angry with me, They made me keeper of the vineyards, My vineyard — my own — I have not kept.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Declare to me, thou whom my soul hath loved, Where thou delightest, Where thou liest down at noon, For why am I as one veiled, By the ranks of thy companions?
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
If thou knowest not, O fair among women, Get thee forth by the traces of the flock, And feed thy kids by the shepherds' dwellings!
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
To my joyous one in chariots of Pharaoh, I have compared thee, my friend,
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Comely have been thy cheeks with garlands, Thy neck with chains.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Garlands of gold we do make for thee, With studs of silver!
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
While the king [is] in his circle, My spikenard hath given its fragrance.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
A bundle of myrrh [is] my beloved to me, Between my breasts it lodgeth.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
A cluster of cypress [is] my beloved to me, In the vineyards of En-Gedi!
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
Lo, thou [art] fair, my friend, Lo, thou [art] fair, thine eyes [are] doves!
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Lo, thou [art] fair, my love, yea, pleasant, Yea, our couch [is] green,
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
The beams of our houses [are] cedars, Our rafters [are] firs, I [am] a rose of Sharon, a lily of the valleys!

< Nyimbo ya Solomoni 1 >