< Rute 4 >

1 Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.
Booz fue a la puerta de la ciudad, y se sentó allí. El redentor de la familia que Booz había mencionado pasó por allí, así que Booz le dijo: “Ven aquí, amigo, y siéntate”. El hombre se acercó y se sentó.
2 Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.
Entonces Booz seleccionó a diez de los ancianos del pueblo y les pidió que se sentaran allí con ellos.
3 Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja.
Booz le dijo al redentor de la familia: “Noemí, que ha regresado del país de Moab, está vendiendo el terreno que pertenecía a Elimelec, nuestro pariente.
4 Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”
Hedecidido decírtelo por si quieres comprarlo aquí, en presencia de estos ancianos del pueblo. Si quieres redimirla, adelante. Pero si no quieres, dímelo para que lo sepa, porque tú eres el primero en la fila para canjearlo, y yo soy el siguiente”. “Quiero redimirla”, dijo el redentor de la familia.
5 Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”
“Cuando compras la tierra a Noemí, también adquieres a Rut la moabita, la viuda de Mahlón, para poder casarte con ella y tener hijos con ella para asegurar la continuidad del linaje del hombre”, explicó Booz.
6 Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”
“Pues entonces no puedo hacerlo”, respondió el redentor de la familia. “Si la redimiera, eso podría poner en peligro lo que ya poseo. Redímela tú, porque yo no puedo”.
7 (Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).
(Ahora bien, en aquellos tiempos era costumbre en Israel confirmar la acción del redentor familiar, el traspaso de la propiedad o cualquier asunto legal similar, quitándose una sandalia y entregándola. Esta era la forma de validar una transacción en Israel).
8 Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.
Así que el redentor familiar se quitó la sandalia y le dijo a Booz: “Cómprala tú”.
9 Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni.
Entonces Booz dijo a los ancianos y a todo el pueblo presente: “Ustedes son testigos de que hoy he comprado a Noemí todo lo que pertenecía a Elimelec, Mahlón y Quelión.
10 Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”
También he adquirido como esposa a Rut la moabita, viuda de Mahlón. Al tener hijos que puedan heredar sus bienes, su nombre se mantendrá vivo en su familia y en su ciudad natal. Ustedes son testigos de esto hoy”.
11 Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu.
Los ancianos y todo el pueblo presente en la puerta de la ciudad dijeron: “Sí, somos testigos. Que el Señor haga que la mujer que viene a tu casa sea como Raquel y Lea, que entre ambas dieron a luz al pueblo de Israel. Que seas próspera en Efrata y famosa en Belén.
12 Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”
Que tu descendencia que el Señor te da a través de esta joven llegue a ser como la descendencia de Fares, el hijo que Tamar dio a Judá”.
13 Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.
Booz se llevó a Rut a su casa y ella se convirtió en su esposa. Se acostó con ella, y el Señor dispuso que quedara embarazada, y dio a luz un hijo.
14 Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli.
Las mujeres de la ciudad se acercaron a Noemí y le dijeron: “Alaba al Señor, porque hoy no te ha dejado sin redentor de familia al darte este nieto que tendrá gran nombre en todo Israel.
15 Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”
Él te dará una nueva vida y te mantendrá en tu vejez, porque tu nuera, que te ama y que es mejor que siete hijos para ti, lo ha dado a luz”.
16 Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.
Noemí cogió al niño y lo abrazó. Lo cuidó como a su propio hijo.
17 Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.
Las vecinas le pusieron el nombre de Obed diciendo: “¡Noemí tiene ahora un hijo!” Era el padre de Jesé, que fue el padre de David.
18 Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi: Perezi anali abambo a Hezironi.
Este es el linaje de Fares: Fares fue el padre de Jezrón.
19 Hezironi anali abambo a Ramu, Ramu anali abambo a Aminadabu,
Jezron fue el padre de Ram. Ram fue el padre de Aminadab.
20 Aminadabu abambo a Naasoni, Naasoni anali abambo a Salimoni,
Aminadab fue el padre de Naasón. Naasón fue el padre de Salmón.
21 Salimoni abambo a Bowazi, Bowazi abambo a Obedi.
Salmón fue el padre de Booz. Booz fue el padre de Obed.
22 Obedi anali abambo a Yese, ndipo Yese anali abambo a Davide.
Obed fue el padre de Isaí. Isaí fue el padre de David.

< Rute 4 >