< Rute 4 >
1 Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.
Now Boaz went up to the gate, and sat him down there; and, behold, the near kinsman of whom Boaz spoke came by; unto whom he said: 'Ho, such a one! turn aside, sit down here.' And he turned aside, and sat down.
2 Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.
And he took ten men of the elders of the city, and said: 'Sit ye down here.' And they sat down.
3 Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja.
And he said unto the near kinsman: 'Naomi, that is come back out of the field of Moab, selleth the parcel of land, which was our brother Elimelech's;
4 Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”
and I thought to disclose it unto thee, saying: Buy it before them that sit here, and before the elders of my people. If thou wilt redeem it, redeem it; but if it will not be redeemed, then tell me, that I may know; for there is none to redeem it beside thee; and I am after thee.' And he said: 'I will redeem it.'
5 Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”
Then said Boaz: 'What day thou buyest the field of the hand of Naomi — hast thou also bought of Ruth the Moabitess, the wife of the dead, to raise up the name of the dead upon his inheritance?'
6 Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”
And the near kinsman said: 'I cannot redeem it for myself, lest I mar mine own inheritance; take thou my right of redemption on thee; for I cannot redeem it.' —
7 (Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).
Now this was the custom in former time in Israel concerning redeeming and concerning exchanging, to confirm all things: a man drew off his shoe, and gave it to his neighbour; and this was the attestation in Israel. —
8 Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.
So the near kinsman said unto Boaz: 'Buy it for thyself.' And he drew off his shoe.
9 Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni.
And Boaz said unto the elders, and unto all the people: 'Ye are witnesses this day, that I have bought all that was Elimelech's, and all that was Chilion's and Mahlon's, of the hand of Naomi.
10 Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”
Moreover Ruth the Moabitess, the wife of Mahlon, have I acquired to be my wife, to raise up the name of the dead upon his inheritance, that the name of the dead be not cut off from among his brethren, and from the gate of his place; ye are witnesses this day.'
11 Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu.
And all the people that were in the gate, and the elders, said: 'We are witnesses. The LORD make the woman that is come into thy house like Rachel and like Leah, which two did build the house of Israel; and do thou worthily in Ephrath, and be famous in Beth-lehem;
12 Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”
and let thy house be like the house of Perez, whom Tamar bore unto Judah, of the seed which the LORD shall give thee of this young woman.'
13 Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.
So Boaz took Ruth, and she became his wife; and he went in unto her, and the LORD gave her conception, and she bore a son.
14 Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli.
And the women said unto Naomi: 'Blessed be the LORD, who hath not left thee this day without a near kinsman, and let his name be famous in Israel.
15 Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”
And he shall be unto thee a restorer of life, and a nourisher of thine old age; for thy daughter-in-law, who loveth thee, who is better to thee than seven sons, hath borne him.'
16 Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.
And Naomi took the child, and laid it in her bosom, and became nurse unto it.
17 Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.
And the women her neighbours gave it a name, saying: 'There is a son born to Naomi'; and they called his name Obed; he is the father of Jesse, the father of David.
18 Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi: Perezi anali abambo a Hezironi.
Now these are the generations of Perez: Perez begot Hezron;
19 Hezironi anali abambo a Ramu, Ramu anali abambo a Aminadabu,
and Hezron begot Ram, and Ram begot Amminadab;
20 Aminadabu abambo a Naasoni, Naasoni anali abambo a Salimoni,
and Amminadab begot Nahshon, and Nahshon begot Salmon;
21 Salimoni abambo a Bowazi, Bowazi abambo a Obedi.
and Salmon begot Boaz, and Boaz begot Obed;
22 Obedi anali abambo a Yese, ndipo Yese anali abambo a Davide.
and Obed begot Jesse, and Jesse begot David.