< Rute 4 >

1 Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.
And Boaz went up to the gate, and sat down there. And behold, he that had the right of redemption, of whom Boaz had spoken, came by. And he said, Thou, such a one, turn aside, sit down here. And he turned aside and sat down.
2 Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.
And he took ten men of the elders of the city, and said, Sit down here. And they sat down.
3 Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja.
And he said to him that had the right of redemption: Naomi, who is come back out of the country of Moab, sells the allotment that was our brother Elimelech's.
4 Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”
And I thought I would apprise thee of it and say, Buy [it] in the presence of the inhabitants, and in the presence of the elders of my people. If thou wilt redeem [it], redeem; but if thou wilt not redeem, tell me, that I may know; for there is none to redeem besides thee; and I am after thee. And he said, I will redeem [it].
5 Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”
And Boaz said, On the day thou buyest the field of the hand of Naomi, thou must buy [it] also of Ruth the Moabitess, the wife of the dead, to raise up the name of the dead upon his inheritance.
6 Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”
And he that had the right of redemption said, I cannot redeem [it] for myself, lest I mar mine own inheritance. Redeem thou for thyself what I should redeem, for I cannot redeem [it].
7 (Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).
Now this [was the custom] in former time in Israel concerning redemption and concerning exchange, to confirm the whole matter: a man drew off his sandal, and gave it to his neighbour, and this was the [mode of] attestation in Israel.
8 Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.
And he that had the right of redemption said to Boaz, Buy for thyself; and he drew off his sandal.
9 Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni.
And Boaz said to the elders and all the people, Ye are witnesses this day, that I have bought all that was Elimelech's, and all that was Chilion's and Mahlon's, of the hand of Naomi;
10 Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”
moreover Ruth the Moabitess, the wife of Mahlon, have I purchased to be my wife, to raise up the name of the dead upon his inheritance, that the name of the dead be not cut off from among his brethren and from the gate of his place: ye are witnesses this day.
11 Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu.
And all the people that were in the gate and the elders said, [We are] witnesses. Jehovah make the woman that cometh into thy house like Rachel and like Leah, which two did build the house of Israel; and acquire power in Ephratah, and make thyself a name in Bethlehem;
12 Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”
and let thy house become like the house of Pherez, whom Tamar bore to Judah, of the seed which Jehovah shall give thee of this young woman.
13 Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.
And Boaz took Ruth, and she became his wife; and he went in unto her, and Jehovah gave her conception, and she bore a son.
14 Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli.
And the women said to Naomi, Blessed be Jehovah who hath not left thee this day without one that has the right of redemption, and may his name be famous in Israel!
15 Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”
And he shall be to thee a restorer of thy life, and a nourisher of thine old age; for thy daughter-in-law who loves thee, who is better to thee than seven sons, has borne him.
16 Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.
And Naomi took the child, and laid it in her bosom, and became nurse to it.
17 Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.
And the women [her] neighbours gave it a name, saying, There is a son born to Naomi. And they called his name Obed. He is the father of Jesse, the father of David.
18 Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi: Perezi anali abambo a Hezironi.
Now these are the generations of Pherez. Pherez begot Hezron,
19 Hezironi anali abambo a Ramu, Ramu anali abambo a Aminadabu,
and Hezron begot Ram, and Ram begot Amminadab,
20 Aminadabu abambo a Naasoni, Naasoni anali abambo a Salimoni,
and Amminadab begot Nahshon, and Nahshon begot Salmon,
21 Salimoni abambo a Bowazi, Bowazi abambo a Obedi.
and Salmon begot Boaz, and Boaz begot Obed,
22 Obedi anali abambo a Yese, ndipo Yese anali abambo a Davide.
and Obed begot Jesse, and Jesse begot David.

< Rute 4 >