< Rute 4 >
1 Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.
And Booz went up to the gate, and sat there; and behold, the relative passed by, of whom Booz spoke: and Booz said to him, Turn aside, sit down here, such a one: and he turned aside and sat down.
2 Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.
And Booz took ten men of the elders of the city, and said, Sit you here; and they sat down.
3 Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja.
And Booz said to the relative, [The matter regards] the portion of the field which was our brother Elimelech's which was given to Noemin, now returning out of the land of Moab;
4 Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”
and I said, I will inform you, saying, Buy it before those that sit, and before the elders of my people: if you will redeem it, redeem it, but if you will not redeem it, tell me, and I shall know; for there is no one beside you to do the office of a kinsman, and I am after you: and he said, I am [here], I will redeem it.
5 Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”
And Booz said, In the day of your buying the field of the hand of Noemin and of Ruth the Moabitess the wife of the deceased, you must also buy her, so as to raise up the name of the dead upon his inheritance.
6 Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”
And the kinsman said, I shall not be able to redeem it for myself, lest I mar my own inheritance; do you redeem my right for yourself, for I shall not be able to redeem [it].
7 (Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).
And this [was] in former time the ordinance in Israel for redemption, and for a bargain, to confirm every word: A man loosed his shoe, and gave it to his neighbour that redeemed his right; and this was a testimony in Israel.
8 Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.
And the kinsman said to Booz, Buy my right for yourself: and he took off his shoe and gave it to him.
9 Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni.
And Booz said to the elders and to all the people, You [are] this day witnesses, that I have bought all that was Elimelech's, and all that belonged to Chelaion and Maalon, of the hand of Noemin.
10 Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”
Moreover I have bought for myself for a wife Ruth the Moabitess, the wife of Maalon, to raise up the name of the dead upon his inheritance; so the name of the dead shall not be destroyed from amongst his brethren, and from the tribe of his people: you [are] this day witnesses.
11 Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu.
And all the people who were in the gate said, [We are] witnesses: and the elders said, The Lord make your wife who goes into your house, as Rachel and as Lia, who both [together] built the house of Israel, and wrought mightily in Ephratha, and there shall be a name [to you] in Bethleem.
12 Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”
And let your house be as the house of Phares, whom Thamar bore to Juda, of the seed which the Lord shall give you of this handmaid.
13 Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.
And Booz took Ruth, and she became his wife, and he went in to her; and the Lord gave her conception, and she bore a son.
14 Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli.
And the woman said to Noemin, Blessed [is] the Lord, who has not suffered a redeemer to fail you this day, even to make your name famous in Israel.
15 Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”
And he shall be to you a restorer of your soul, and one to cherish your old age; for your daughter-in-law which has loved you, who is better to you than seven sons, has born him.
16 Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.
And Noemin took the child and laid it in her bosom, and became a nurse to it.
17 Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.
And the neighbours gave it a name, saying, A son has been born to Noemin; and they called his name Obed; this [is] the father of Jessae the father of David.
18 Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi: Perezi anali abambo a Hezironi.
And these [are] the generations of Phares: Phares begot Esrom:
19 Hezironi anali abambo a Ramu, Ramu anali abambo a Aminadabu,
Esrom begot Aram; and Aram begot Aminadab.
20 Aminadabu abambo a Naasoni, Naasoni anali abambo a Salimoni,
And Aminadab begot Naasson; and Naasson begot Salmon.
21 Salimoni abambo a Bowazi, Bowazi abambo a Obedi.
And Salmon begot Booz; and Booz begot Obed.
22 Obedi anali abambo a Yese, ndipo Yese anali abambo a Davide.
And Obed begot Jessae; and Jessae begot David.