< Rute 4 >
1 Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.
Hatnavah, Boaz teh khopui longkha koe a cei teh a tahung. Paduem a dei e pacanaw ni a cei e a hmu navah, a kamlang teh, api nang maw, tahung leih atipouh e patetlah a kamlang teh a tahung.
2 Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.
Hahoi, khopui thung e kacuenaw tami hra touh a kaw teh, hi tahung atipouh e patetlah a tahung.
3 Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja.
A pacanaw ni hai Moab kho hoi ka tho e Naomi ni maimae hmau, Elimelek e talai a yo han dawkvah,
4 Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”
nang na thai sak. Khocanaw, kaimae pacanaw dawk hoi kacuenaw e hmalah ran leih telah dei hanlah pouknae ka tawn. Nang ni ratang na ngai pawiteh ratang leih. Na ratang ngai hoehpawiteh kai koe bout dei lawih. Kai laipalah alouke ka ratang thai e awm hoeh. Nange na hnukkhu lah kai ka o atipouh navah paca ni kai ni ka ratang han telah ati.
5 Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”
Boaz ni hai hote laikawk hah Naomi koe rannae hnin navah kadout e râw lahoi a minhmai khet hanelah a yu Moab napui Ruth hah a ran sin telah ati navah,
6 Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”
A paca ni kai ni kama hanlah ka ratang thai mahoeh. Ka ratang pawiteh ka râw raphoe e lah ao han ti a lakueng. Kai ni ka ratang hoeh toung dawkvah kaie ratangthainae hah, nama hanlah ratang lawih telah atipouh.
7 (Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).
Isarelnaw e singyoe patetlah ratangnae, hno kâthung e a kangning thai nahanlah buet touh ni amae khokkhawm a rading vaiteh buet touh koe ouk a hnawng. Hottelah, sak e lahoi, Isarel miphunnaw koe panuekhainae teh acak.
8 Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.
Hatdawkvah, a paca ni, ma hanelah ran leih telah Boaz koe a dei pouh e patetlah Boaz ni amae khokkhawm teh a rading.
9 Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni.
Boaz ni hai Elimelek e hno, Khilion e hno hoi Mahlon e hnonaw pueng Naomi kut dawk e ka ran teh,
10 Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”
Kadout e min hah ahnie hmaunawngha thung hoi thoseh, a onae khopui longkha koehoi thoseh ahnie râw lahoi a min pâpout hoeh nahanelah, Mahlon e a yu Moab napui Ruth heh ka yu lah ao thai nahan, ka ran tie hah nangmanaw teh sahnin kapanuekkhaikung lah na o awh.
11 Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu.
Longkha koe kaawm e kacuenaw, taminaw pueng ni kapanuekkhaikung lah ao awh. Na im ka tho e napui ni Isarel miphun kangdout sak e napui kahni touh teh kaimouh koe, Rachel hoi Leah patetlah ao nahan, BAWIPA ni sak lawiseh. Nang hai Epharath kho dawk thao thasainae hoi na kawi vaiteh, Bethlehem khopui dawk min kamthang lawiseh,
12 Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”
Karoung takhang e hete napui koe, Cathut ni a poe hane cati lahoi, nange catounnaw teh, Judah e a yu Tamar ni a khe e Parez catoun patetlah awm naseh telah a dei awh.
13 Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.
Boaz ni Ruth a paluen teh, a okhai navah Cathut lungmanae lahoi ca a von teh ca tongpa a khe.
14 Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli.
Napuinaw ni hai Naomi koevah nang na khenyawn hanelah na miphun ka cettakhai hoeh e Cathut yawhawinae awmseh. Atu na khe e na miphun heh Isarel miphun dawk kamthangnae awm lawiseh,
15 Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”
Ahni teh na hringnae ka khenyawn e tami, na matawng navah na ka kawk e tami lah awmseh. Nang lung na ka pataw e tawngpa sari touh hlak hai hoe kahawi e na langa ni ca tongpa a khe toe atipouh awh.
16 Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.
Naomi ni camo hah a la teh, a tawm teh a okhai
17 Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.
Imri e napuinaw ni hai Naomi ni a ca tongpa a khe ati awh teh, hote camo teh Obed telah min a phung awh. Obed capa Jesi, Jesi capa Devit.
18 Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi: Perezi anali abambo a Hezironi.
Perez e catounnaw teh: Perez capa Hezron,
19 Hezironi anali abambo a Ramu, Ramu anali abambo a Aminadabu,
Hezron capa Ram, Ram capa Amminadab,
20 Aminadabu abambo a Naasoni, Naasoni anali abambo a Salimoni,
Amminadab capa Nahshon, Nahshon capa Salmon,
21 Salimoni abambo a Bowazi, Bowazi abambo a Obedi.
Salmon capa Boaz, Boaz capa Obed,
22 Obedi anali abambo a Yese, ndipo Yese anali abambo a Davide.
Obed capa Jesi, Jesi capa Devit lah ao.