< Rute 4 >
1 Nthawi yomweyo Bowazi anapita ku chipata cha mzinda ndi kukhala pansi kumeneko pabwalo losonkhanira. Tsono anangoona wachibale woyenera kulowa chokolo uja akufika. Ndipo Bowazi anati, “Patukirani kuno, bwenzi langa. Mubwere mudzakhale apa.” Choncho anapatuka nakakhala pansi.
И Вооз възлезе на портата и седна там; и, ето, минаваше близкият сродник, за когото беше говорил Вооз. И рече: Господине, свърни, седни тук. И той свърна и седна.
2 Bowazi anayitananso akuluakulu khumi a mu mzindamo nati, “Dzakhaleni pansi apa,” ndipo anadzakhala pansi.
Тогава Вооз събра десет мъже от градските старейшини и рече: Седнете тук. И те седнаха.
3 Kenaka anamuwuza oyenera kulowa chokolo uja kuti, “Naomi amene wabwera kuchoka ku Mowabu akugulitsa malo amene anali a malemu Elimeleki, mʼbale wathu uja.
После рече на сродника: Ноемин, която се върна от Моавската земя, продава нивата, дяла, който принадлежеше на брата ни Елимелеха;
4 Choncho ndinaganiza zokuwuza zimenezi kuti ugule mundawu pamaso pa anthu amene ali panowa, ndi pamaso pa akuluakulu mwa abale athu. Ngati ukufuna kuwuwombola, uwombole. Koma ngati sukufuna, undiwuze kuti ndidziwe, pakuti palibe wina angawuwombole koma iweyo, ndipo pambuyo pa iwe pali ine.” Iye anati, “Ine ndidzawuwombola.”
а аз рекох да ти известя и да ти кажа: Купи го пред седящите тука, пред старейшините на людете ми. Ако щеш да го откупиш като сродник, откупи го; но, ако не щеш да го откупиш, кажи ми, за да зная; защото освен тебе, няма друг да го откупи, като сродник; и аз съм подир тебе. И той рече: Аз ще го откупя.
5 Tsono Bowazi anati, “Tsiku limene ukagule mundawo kwa Naomi, udzatenganso Rute Mmowabu, mkazi wamasiye uja, kuti dzina la malemu lisungike pa cholowa chake.”
И рече Вооз: В деня, когато купиш нивата от ръката на Ноемин, трябва да я купиш и от моавката Рут, жена на умрелия, за да възстановиш името на умрелия над наследството му.
6 Pamenepo wachibaleyo anati, “Sindingathe kuwuwombola mundawu kuti ukhale wanga, kuopa kuti kutaya cholowa changa. Mugule ndinu. Ine sindingathe.”
Тогава сродникът рече: Не мога да изпълня длъжността на сродник, да не би да напакостя на своето си наследство; ти приеми върху себе си моето право да откупя, защото не мога да откупя нивата.
7 (Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli).
А в старо време, за да се утвърди всяко дело по откупване и размяна в Израиля, ето що беше обичаят: човекът изуваше обувката си, та я даваше на ближния си: и така се свидетелствуваше в Израиля.
8 Choncho wachibale uja atawuza Bowazi kuti, “Gulani ndinu mundawu.” Iye anavula nsapato yake namupatsa Bowazi.
За това, сродникът като каза на Вооза: Купи го ти за себе си, изу си обувката.
9 Ndipo Bowazi anawuza akuluakuluwo ndi anthu onse aja kuti, “Nonsenu ndinu mboni lero, kuti ine ndagula kwa Naomi zonse zimene zinali za malemu Elimeleki, zonse zimene zinali za malemu Kiliyoni ndiponso za malemu Maloni.
Тогава Вооз каза на старейшините и на всичките люде: Днес сте свидетели, че купувам от ръката на Ноемин всичко, що беше Елимелехово и всичко що беше Хелеоново и Маалоново.
10 Ndatenganso Rute Mmowabu uja mkazi wa malemu Maloni, kuti akhale mkazi wanga, kuti dzina la malemu Maloni lisungike pa cholowa chake, ndipo lisafafanizike pakati pa abale ake ngakhalenso mʼmudzi mwake. Nonsenu ndinu mboni lero lino.”
А още и моавката Рут Маалоновата жена, придобих за жена, за да възстановя името на умрелия над наследството му, за да се не изличи името на умрелия измежду братята му и из града на обитаването му; вие сте свидетели днес.
11 Ndipo akuluakulu aja ndi anthu onse amene anali pa chipata anati, “Ife ndife mboni, ndipo Yehova amusandutsa mkazi amene akudzalowa mʼnyumba yakoyu kuti akhale ngati Rakele ndi Leya, amene anamanga banja la Israeli. Ukhale munthu wosasowa kanthu mu Efurata ndi munthu wotchuka mu Betelehemu.
И всичките люде, които бяха в портата, и старейшините рекоха: Свидетели сме. Господ да направи жената, която влиза в дома ти, като Рахил и като Лия, двете, които са съградили Израилевия дом; и да станеш силен в Ефрата, и да бъдеш знаменит във Витлеем;
12 Ana amene Yehova adzakupatsa mwa mkaziyu adzamange banja lako kukhala la Perezi, amene Tamara anamubalira Yuda.”
и от потомството, което Господ ще ти даде от тая млада жена, нека бъде домът ти като дома на Фареса, когото Тамар роди на Юда.
13 Choncho Bowazi anakwatira Rute. Yehova anamudalitsa nakhala ndi pakati, ndipo anabereka mwana wamwamuna.
И така, Вооз взе Рут, и тя му стана жена; и като влезе при нея, Господ й даде зачатие, и тя роди син.
14 Ndipo amayi osiyanasiyana anati kwa Naomi. “Alemekezeke Yehova, amene lero lino sanakusiyeni nokha wopanda wachibale. Mwanayu dzina lake likhale lotchuka mu Israeli.
И жените казаха на Ноемин: Благословен Господ, Който днес не те остави без сродник; нека бъде прочуто Името Му в Израиля.
15 Mwanayo adzakupatseni moyo watsopano ndi kukuthandizani pa ukalamba wanu. Inde, mpongozi wanu amene amakukondani, amenenso waonetsa kuti ali wopambana kwa inu kuposa ana aamuna asanu ndi awiri, ndiye wakubalirani mwanayu.”
Тоя син ще ти бъде обнова на живота и прехрана в старините ти; защото го роди снаха ти, която те обича, която е за тебе по-желателна от седем сина.
16 Kenaka Naomi anatenga mwanayo namufukata ndipo anakhala mlezi.
И Ноемин взе детето и тури го в пазухата си, и стана му кърмилница.
17 Amayi achinansi ake anati, “Naomi ali ndi mwana wamwamuna.” Ndipo anamutcha dzina lake Obedi. Iye anali abambo a Yese abambo ake a Davide.
И съседките ме дадоха име казвайки: Син се роди на Ноемин. И рекоха го Овид; той е баща на Есея, Давидовия баща.
18 Izi tsono ndizo zidzukulu za Perezi: Perezi anali abambo a Hezironi.
И ето Фаресовото родословие: Фарес роди Есрона,
19 Hezironi anali abambo a Ramu, Ramu anali abambo a Aminadabu,
Есрон роди Арама, Арам роди Аминадава,
20 Aminadabu abambo a Naasoni, Naasoni anali abambo a Salimoni,
Аминадав роди Наасона, Наасон роди Салмона,
21 Salimoni abambo a Bowazi, Bowazi abambo a Obedi.
Салмон роди Вооза, Вооз роди Овида,
22 Obedi anali abambo a Yese, ndipo Yese anali abambo a Davide.
Овид роди Есея, а Есей роди Давида.