< Rute 3 >
1 Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
Et Naomi, sa belle-mère, lui dit: Ma fille, ne te chercherai-je pas un asile, afin que tu sois heureuse?
2 Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
Et maintenant, Booz, avec les servantes de qui tu as été, n'est-il pas notre parent? Voici, il vannera cette nuit les orges qui sont dans son aire.
3 Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
Lave-toi, et oins-toi, et mets sur toi ton manteau, et descends dans l'aire; mais ne te fais point connaître à cet homme, jusqu'à ce qu'il ait achevé de manger et de boire.
4 Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
Et quand il se couchera, sache le lieu où il couche, puis entre, et découvre ses pieds, et te couche; alors il te dira ce que tu auras à faire.
5 Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
Et elle lui répondit: Je ferai tout ce que tu me dis.
6 Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
Elle descendit donc à l'aire, et fit tout ce que sa belle-mère lui avait commandé.
7 Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
Et Booz mangea et but, et son cœur fut heureux, et il vint se coucher au bout d'un tas de gerbes. Alors elle vint tout doucement, et découvrit ses pieds, et se coucha.
8 Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
Et au milieu de la nuit, cet homme-là eut peur; il se pencha, et voici, une femme était couchée à ses pieds.
9 Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
Alors il lui dit: Qui es-tu? Et elle répondit: Je suis Ruth, ta servante. Étends le pan de ta robe sur ta servante; car tu as droit de rachat.
10 Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
Et il dit: Ma fille, que l'Éternel te bénisse! Cette dernière bonté que tu me témoignes est plus grande que la première, de n'être point allée après les jeunes gens, pauvres ou riches.
11 Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
Maintenant donc, ma fille, ne crains point, je ferai pour toi tout ce que tu me diras; car toute la porte de mon peuple sait que tu es une femme vertueuse.
12 Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
Et maintenant, il est très vrai que j'ai droit de rachat; mais il y en a un autre, qui est plus proche que moi.
13 Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
Passe ici cette nuit; et, au matin, si cet homme veut user du droit de rachat envers toi, à la bonne heure, qu'il en use; mais s'il ne lui plaît pas de te racheter, moi je te rachèterai; l'Éternel est vivant! Reste couchée jusqu'au matin.
14 Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
Elle demeura donc couchée à ses pieds, jusqu'au matin; et elle se leva avant qu'on pût se reconnaître l'un l'autre. Et Booz dit: Qu'on ne sache pas qu'une femme est entrée dans l'aire.
15 Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
Il lui dit encore: Donne-moi le manteau qui est sur toi, et tiens-le. Et elle le tint, et il mesura six mesures d'orge, qu'il chargea sur elle; puis il rentra dans la ville.
16 Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
Puis Ruth revint chez sa belle-mère, qui lui dit: Qui es-tu, ma fille? Et elle lui déclara tout ce que cet homme avait fait pour elle.
17 Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
Et elle dit: Il m'a donné ces six mesures d'orge; car il m'a dit: Tu ne retourneras point à vide auprès de ta belle-mère.
18 Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”
Et Naomi dit: Ma fille, reste ici jusqu'à ce que tu saches comment la chose tournera; car cet homme ne se donnera point de repos qu'il n'ait aujourd'hui achevé cette affaire.