< Rute 3 >

1 Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
Et Naomi, sa belle-mère, lui dit: Ma fille, ne te chercherai-je pas du repos, afin que tu sois heureuse?
2 Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
Et maintenant, Boaz, avec les jeunes filles duquel tu as été, n’est-il pas de nos amis? Voici, il vanne cette nuit les orges dans l’aire.
3 Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
Lave-toi donc, et oins-toi, et mets sur toi tes habits, et descends dans l’aire; ne te fais pas connaître à l’homme, jusqu’à ce qu’il ait achevé de manger et de boire.
4 Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
Et lorsqu’il se couchera, alors tu remarqueras le lieu où il se couche, et tu entreras, et tu découvriras ses pieds, et tu te coucheras; et lui, te fera connaître ce que tu auras à faire.
5 Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
Et elle lui dit: Tout ce que tu as dit, je le ferai.
6 Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
Et elle descendit à l’aire, et fit selon tout ce que sa belle-mère lui avait commandé.
7 Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
Et Boaz mangea et but, et son cœur devint gai, et il alla se coucher au bout du tas des gerbes. Et elle vint tout doucement, et découvrit ses pieds, et se coucha.
8 Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
Et il arriva au milieu de la nuit, que l’homme eut peur et se tourna; et voici, une femme était couchée à ses pieds.
9 Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
Et il dit: Qui es-tu? Et elle dit: Je suis Ruth, ta servante; et étends ton aile sur ta servante, car tu as le droit de rachat.
10 Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
Et il dit: Bénie sois-tu de l’Éternel, ma fille! Tu as montré plus de bonté à la fin qu’au commencement, en ce que tu n’es pas allée après les jeunes hommes, pauvres ou riches.
11 Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
Et maintenant, ma fille, ne crains pas; tout ce que tu [me] dis, je le ferai pour toi; car toute la porte de mon peuple sait que tu es une femme vertueuse.
12 Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
Et maintenant, il est bien vrai que j’ai le droit de rachat, toutefois il y en a un qui a le droit de rachat, [et qui est] plus proche que moi.
13 Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
Passe [ici] la nuit; et s’il arrive que, le matin, il veuille te racheter, c’est bien! qu’il le fasse; et s’il ne lui plaît pas de te racheter, l’Éternel est vivant que je le ferai, moi! Reste couchée jusqu’au matin.
14 Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
Et elle resta couchée là à ses pieds jusqu’au matin; et elle se leva avant qu’on puisse se reconnaître l’un l’autre. Et il dit: Qu’on ne sache pas qu’une femme est venue dans l’aire.
15 Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
Et il [lui] dit: Donne le manteau qui est sur toi, et tiens-le. Et elle le tint, et il mesura six [mesures] d’orge, et les mit sur elle; et il entra dans la ville.
16 Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
Et elle vint vers sa belle-mère; et celle-ci dit: Qui es-tu, ma fille? Et elle lui raconta tout ce que l’homme avait fait pour elle;
17 Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
et elle dit: Il m’a donné ces six [mesures] d’orge; car il m’a dit: Tu n’iras pas à vide vers ta belle-mère.
18 Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”
Et [Naomi] dit: Demeure, ma fille, jusqu’à ce que tu saches comment l’affaire tournera; car l’homme n’aura pas de repos qu’ il n’ait terminé l’affaire aujourd’hui.

< Rute 3 >