< Rute 2 >

1 Naomi anali ndi mʼbale wake wolemera kwambiri wochokera ku banja la mwamuna wake Elimeleki, dzina lake Bowazi.
There was a man in Bethlehem who belonged to the clan of [Naomi’s dead husband], Elimelech. He was rich and well-known/influential. His name was Boaz.
2 Tsiku lina Rute, Mmowabu uja anati kwa Naomi, “Mundilole kuti ndikakunkhe barele ku munda wa munthu aliyense amene akandikomere mtima.” Naomi anati kwa iye, “Pita mwana wanga.”
[One day] Ruth said to Naomi, “Let me go to the fields and pick up the grain left behind by the workers.” Naomi replied, “Go ahead, my daughter.”
3 Choncho Rute ananyamuka kupita kukakunkha ku minda yokololedwa kale. Tsono zinangochitika kuti Rute anafika mʼmunda wa Bowazi, yemwe anali wochokera ku banja la Elimeleki.
So Ruth went to the fields and began to pick up some of the left-over grain. And it happened that she was working in a field that belonged to Boaz, [the man] from the clan of [her dead father-in-law], Elimelech!
4 Posakhalitsa Bowazi anafika kuchokera ku Betelehemu ndipo analonjera okolola aja kuti, “Yehova akhale nanu!” Iwo anayankha kuti, “Yehova akudalitseni.”
Just then, Boaz arrived from Bethlehem. He greeted the men who were harvesting the grain, saying, “I want Yahweh to bless you!” They replied, “We want Yahweh to bless you, [too]!”
5 Bowazi anafunsa kapitawo wake amene ankayangʼanira okolola aja kuti, “Mayi uyo ndi ndani?”
Then Boaz saw Ruth, and asked the (foreman/man in charge of the other workmen), “Whose [daughter] is that young woman?”
6 Kapitawo uja anayankha kuti, “Mayiyu ndi Mmowabu amene anabwera ndi Naomi kuchokera ku dziko la Mowabu.
The foreman replied, “She is the woman from Moab who returned from there with [her mother-in-law] Naomi.
7 Iye anandipempha kuti, ‘Chonde mundilole kuti ndikunkhe barele mʼminda moti akololamo kale.’ Iye wakhala akukunkha kuyambira mmawa mpaka tsopano lino osapuma nʼpangʼono pomwe.”
She said to me, ‘Please let me walk behind the men who are harvesting the grain and pick up some of the grain they leave behind.’ [I gave her permission, and] she went into the field, and she has been working from this morning until now. The only time she did not work was when she rested for a short time in the shelter.”
8 Choncho Bowazi anati kwa Rute, “Tamvera mwana wanga, usapite kukakunkha mʼmunda wina, ndipo usachoke mʼmunda uno. Koma uzitsata adzakazi angawa.
So Boaz went over to Ruth and said to her, “Young lady, listen to me. Don’t go and pick up grain in another field. Do not go away from here. Stay here with my servant girls.
9 Uziyangʼana munda akukolola anyamatawo akamakolola mʼmundamu, ndipo iwe uzitsata pambuyo pawo. Ndawawuza anyamatawo kuti asakuvutitse. Ndipo ukamva ludzu, uzipita ku mitsuko ndi kukamwa madzi amene anyamatawa atunga.”
Watch where the men are harvesting, and follow along behind the [servant] girls. I will tell the men [who are working] not to touch/molest you. And whenever you are thirsty, go and get some water to drink from the jars that the men have filled.”
10 Atamva zimenezi Rute anawerama nazolikitsa nkhope yake pansi. Kenaka anafunsa kuti, “Mwandikomera mtima chotere mlendo ngati ine chifukwa chiyani?”
When he said that, she knelt down in front of him [in respect], with her face touching the ground. She exclaimed, “Why are you acting so kindly toward me, by paying attention to me? [I am not even a Jew; I am] a foreigner!”
11 Bowazi anayankha kuti, “Ine ndawuzidwa zonse zimene wakhala ukuchitira apongozi ako chimwalirire mwamuna wako. Ndamvanso kuti unasiya abambo ndi amayi ako komanso dziko la kwanu ndi kubwera kudzakhala ndi anthu amene sumawadziwa ndi kale lonse.
Boaz replied, “People have told me all about what you have done for your mother-in-law. They told me that you left your parents and your homeland, and you came here to live among people whom you did not know before.
12 Yehova akubwezere pa zimene wachitazi. Yehova Mulungu wa Israeli, amene wabwera pansi pa mapiko ake kuti akuteteze, akupatse mphotho yayikulu.”
I hope/desire that Yahweh will repay you for what you have done. You have put yourself in the care of Yahweh, [like a little bird puts itself] under [its mother’s] wings [MET]. I desire that he will reward you very greatly.”
13 Rute anati, “Mwandikomera mtima, mbuye wanga. Ndipo mwandisangalatsa ndi kundiyankhula mwa chifundo ngakhale sindili mmodzi mwa adzakazi anu.”
She replied, “Sir, I hope you will continue to act kindly toward me. You have comforted/encouraged me, even though I am lower in status than any of your servant girls.”
14 Nthawi ya chakudya cha masana Bowazi anati kwa iye, “Bwera kuno, utenge buledi ndi kusunsa nthongo mu vinyo.” Choncho anakhala pansi pafupi ndi okololawo, ndipo Bowazi anamupatsa chakudya ndi nyama yowotcha. Anadya chilichonse amafuna ndipo chakudya china chinatsalako.
At mealtime, Boaz said to her, “Come over here. Take some bread and dip it in the wine vinegar [and eat it].” Then when she sat down with the men who had been harvesting, he offered her some roasted grain. She ate all the grain she wanted, and had some left over.
15 Atanyamuka kuti azikakunkha, Bowazi analangiza anyamata ake kuti, “Ngakhale mayiyu azikunkha pakati pa mitolo musamuletse ndi kumuchititsa manyazi.
As she stood up to start gathering grain [again], Boaz ordered his workers, “Even if she gathers some grain near the bundles of grain that have been cut, do not scold her.
16 Koma muzimusololerako ngala zina za mʼmitolo ndi kumusiyira kuti azikunkha ndipo musamukalipire.”
Instead, pull out some stalks of grain from the bundles, and leave them on the ground for her to pick up, and do not rebuke her.”
17 Choncho Rute anakunkha mʼmundamo mpaka madzulo. Kenaka anapuntha barele anakunkhayo, ndipo anakwanira pafupifupi makilogalamu khumi.
So Ruth gathered grain in the field until evening. Then she (threshed/beat with a stick) the barley that she had gathered, [to separate the kernels from the stalks], and the barley filled a large basket.
18 Anasenza barele uja kupita naye ku mudzi, nakaonetsa apongozi ake. Kenaka anatulutsa chakudya chimene chinatsalira atakhuta chija ndi kupatsa apongozi ake.
She carried it back to town, and showed to her mother-in-law how much she had gathered. Ruth also showed to her the grain [that was left over after] she had eaten enough from [what Boaz had given her at lunchtime].
19 Apongozi akewo anamufunsa kuti, “Kodi lero unakakunkha kuti? Unakagwira kuti ntchitoyi? Adalitsike munthu amene anakukomera mtimayo.” Ndipo Rute anawuza mpongozi wake za munthu amene ku malo ake anakagwirako ntchito. Iye anati, “Munthuyo dzina lake ndi Bowazi.”
Her mother-in-law asked her, “Where did you gather grain today? In whose [field] did you work? [God will] surely bless the man who was kind to you.” Then Ruth told her about the man in whose field she had been working. She said, “The name of the man [who owns the field] where I worked today is Boaz.”
20 Naomi anati kwa mpongozi wakeyo, “Munthu ameneyu amudalitse Yehova, amene sanasiye kuchitira chifundo anthu amoyo ndi akufa omwe. Anatinso munthu ameneyu ndi mnansi wapaphata. Ndiye ali ndi udindo wotisamalira.”
Naomi said to her daughter-in-law, “I hope/desire that Yahweh will bless him! He has not stopped acting kindly toward [us, who are still] living, and to [our husbands] who have died.” Then she added, “That man is a close relative [of Elimelech]; he is one of those who has a responsibility to help those who are his relatives.”
21 Choncho Rute Mmowabuyo anati, “Iye anandiwuzanso kuti, ‘Uzitsata antchito angawa mpaka atamaliza kukolola munda wonse.’”
Then Ruth said, “He also said to me, ‘Stay with my workers until they have finished harvesting all my grain.’”
22 Naomi anati kwa Rute mpongozi wake, “Kuli bwino mwana wanga kuti uzipita ndi adzakazi ake kuopa kuti mʼmunda wa munthu wina angakuvute.”
Naomi replied, “My daughter, it will be good for you to go [to his field] with his [servant] girls, because if you go to someone else’s field, someone might harm/molest you.”
23 Choncho Rute ankatsatira adzakazi a Bowazi namakunkha mpaka anthu atamaliza kudula barele ndi tirigu. Ndipo amakhalabe ndi mpongozi wakeyo.
So Ruth stayed close to Boaz’s [servant] girls [while she was working]. She gathered stalks of grain until the barley harvest and the wheat harvest were finished. During that time she lived with Naomi.

< Rute 2 >