< Rute 2 >

1 Naomi anali ndi mʼbale wake wolemera kwambiri wochokera ku banja la mwamuna wake Elimeleki, dzina lake Bowazi.
And Na'omi had a kinsman of her husband's, a mighty, valiant man, of the family of Elimelech, whose name was Bo'az.
2 Tsiku lina Rute, Mmowabu uja anati kwa Naomi, “Mundilole kuti ndikakunkhe barele ku munda wa munthu aliyense amene akandikomere mtima.” Naomi anati kwa iye, “Pita mwana wanga.”
And Ruth the Moabitess said unto Na'omi, Let me go, I pray thee, into the field, and glean ears of corn after him in whose eyes I shall find grace. And she said unto her, Go, my daughter.
3 Choncho Rute ananyamuka kupita kukakunkha ku minda yokololedwa kale. Tsono zinangochitika kuti Rute anafika mʼmunda wa Bowazi, yemwe anali wochokera ku banja la Elimeleki.
And she went, and came, and gleaned in the field after the reapers; and the accident happened to her, that it was a part of the field belonging unto Bo'az, who was of the family of Elimelech.
4 Posakhalitsa Bowazi anafika kuchokera ku Betelehemu ndipo analonjera okolola aja kuti, “Yehova akhale nanu!” Iwo anayankha kuti, “Yehova akudalitseni.”
And, behold, Bo'az came from Beth-lechem, and he said unto the reapers, The Lord be with you. And they said unto him, May the Lord bless thee.
5 Bowazi anafunsa kapitawo wake amene ankayangʼanira okolola aja kuti, “Mayi uyo ndi ndani?”
Then said Bo'az unto his young man that was appointed over the reapers, Whose maiden is this?
6 Kapitawo uja anayankha kuti, “Mayiyu ndi Mmowabu amene anabwera ndi Naomi kuchokera ku dziko la Mowabu.
And the young man that was appointed over the reapers answered and said, It is a Moabitish maiden that is returned with Na'omi out of the fields of Moab;
7 Iye anandipempha kuti, ‘Chonde mundilole kuti ndikunkhe barele mʼminda moti akololamo kale.’ Iye wakhala akukunkha kuyambira mmawa mpaka tsopano lino osapuma nʼpangʼono pomwe.”
And she said, Let me glean, I pray you, and gather among the sheaves after the reapers: so she came, and hath remained ever from the morning even until now; it is but a little while that she hath sat down in the house.
8 Choncho Bowazi anati kwa Rute, “Tamvera mwana wanga, usapite kukakunkha mʼmunda wina, ndipo usachoke mʼmunda uno. Koma uzitsata adzakazi angawa.
Then said Bo'az unto Ruth, Hearest thou not, my daughter? Go not to glean in another field, neither go away from this; but keep close company with my own maidens.
9 Uziyangʼana munda akukolola anyamatawo akamakolola mʼmundamu, ndipo iwe uzitsata pambuyo pawo. Ndawawuza anyamatawo kuti asakuvutitse. Ndipo ukamva ludzu, uzipita ku mitsuko ndi kukamwa madzi amene anyamatawa atunga.”
Let thy eyes be on the field which they may reap, and go thou after them; behold, I have charged the young men that they shall not touch thee: and when thou art thirsty, go unto the vessels, and drink of that which the young men may draw.
10 Atamva zimenezi Rute anawerama nazolikitsa nkhope yake pansi. Kenaka anafunsa kuti, “Mwandikomera mtima chotere mlendo ngati ine chifukwa chiyani?”
Thereupon she fell on her face, and bowed herself to the ground, and said unto him, Why have I found grace in thy eyes, that thou shouldst take cognizance of me, seeing I am but a stranger?
11 Bowazi anayankha kuti, “Ine ndawuzidwa zonse zimene wakhala ukuchitira apongozi ako chimwalirire mwamuna wako. Ndamvanso kuti unasiya abambo ndi amayi ako komanso dziko la kwanu ndi kubwera kudzakhala ndi anthu amene sumawadziwa ndi kale lonse.
But Bo'az answered and said unto her, It hath fully been told me, all that thou hast done unto thy mother-in-law after the death of thy husband; and how thou hast forsaken thy father and thy mother, and the land of thy birth, and art come unto a people which thou knewest not yesterday or the day before.
12 Yehova akubwezere pa zimene wachitazi. Yehova Mulungu wa Israeli, amene wabwera pansi pa mapiko ake kuti akuteteze, akupatse mphotho yayikulu.”
May the Lord recompense thy work, and may thy reward be complete from the Lord the God of Israel, under whose wings thou art come to seek shelter.
13 Rute anati, “Mwandikomera mtima, mbuye wanga. Ndipo mwandisangalatsa ndi kundiyankhula mwa chifundo ngakhale sindili mmodzi mwa adzakazi anu.”
Then said she, Let me find grace in thy eyes, my lord; for thou hast comforted me, and because thou hast spoken [kindly] unto the heart of thy handmaid, though I be not like one of thy handmaids.
14 Nthawi ya chakudya cha masana Bowazi anati kwa iye, “Bwera kuno, utenge buledi ndi kusunsa nthongo mu vinyo.” Choncho anakhala pansi pafupi ndi okololawo, ndipo Bowazi anamupatsa chakudya ndi nyama yowotcha. Anadya chilichonse amafuna ndipo chakudya china chinatsalako.
And Bo'az said unto her, At mealtime come near hither, and eat of the bread, and dip thy morsel in the vinegar. And she seated herself beside the reapers: and he reached her parched corn, and she ate, and was satisfied, and had some left.
15 Atanyamuka kuti azikakunkha, Bowazi analangiza anyamata ake kuti, “Ngakhale mayiyu azikunkha pakati pa mitolo musamuletse ndi kumuchititsa manyazi.
Then did she arise to glean: and Bo'az commanded his young men, saying, Even between the sheaves let her glean, and do not cause her to feel any shame;
16 Koma muzimusololerako ngala zina za mʼmitolo ndi kumusiyira kuti azikunkha ndipo musamukalipire.”
And ye shall also draw out some for her from the bundles on purpose, and leave it, that she may glean it, and ye shall not rebuke her.
17 Choncho Rute anakunkha mʼmundamo mpaka madzulo. Kenaka anapuntha barele anakunkhayo, ndipo anakwanira pafupifupi makilogalamu khumi.
So she gleaned in the field until the evening; and when she beat out what she had gleaned, it was about an ephah of barley.
18 Anasenza barele uja kupita naye ku mudzi, nakaonetsa apongozi ake. Kenaka anatulutsa chakudya chimene chinatsalira atakhuta chija ndi kupatsa apongozi ake.
And she took it up, and she went into the city; and her mother-in-law saw what she had gleaned; and she brought forth and gave to her what she had left over after she was satisfied.
19 Apongozi akewo anamufunsa kuti, “Kodi lero unakakunkha kuti? Unakagwira kuti ntchitoyi? Adalitsike munthu amene anakukomera mtimayo.” Ndipo Rute anawuza mpongozi wake za munthu amene ku malo ake anakagwirako ntchito. Iye anati, “Munthuyo dzina lake ndi Bowazi.”
And her mother-in-law said unto her, Where hast thou gleaned today? and where hast thou wrought? may he that took cognizance of thee be blessed. And she told her mother-in-law with whom she had wrought, and said, The name of the man with whom I wrought today is Bo'az.
20 Naomi anati kwa mpongozi wakeyo, “Munthu ameneyu amudalitse Yehova, amene sanasiye kuchitira chifundo anthu amoyo ndi akufa omwe. Anatinso munthu ameneyu ndi mnansi wapaphata. Ndiye ali ndi udindo wotisamalira.”
Then said Na'omi unto her daughter-in-law, Blessed be he unto the Lord, who hath not withheld his kindness from the living and from the dead. And Na'omi said unto her, The man is nearly related unto us, he is one of our next kinsmen.
21 Choncho Rute Mmowabuyo anati, “Iye anandiwuzanso kuti, ‘Uzitsata antchito angawa mpaka atamaliza kukolola munda wonse.’”
And Ruth the Moabitess said, He hath also said unto me, Thou shalt keep close company with my young men, until they have ended all my harvest.
22 Naomi anati kwa Rute mpongozi wake, “Kuli bwino mwana wanga kuti uzipita ndi adzakazi ake kuopa kuti mʼmunda wa munthu wina angakuvute.”
Then said Na'omi unto Ruth her daughter-in-law, It is good, my daughter, that thou go out with his maidens, and that men may not meet with thee in any other field.
23 Choncho Rute ankatsatira adzakazi a Bowazi namakunkha mpaka anthu atamaliza kudula barele ndi tirigu. Ndipo amakhalabe ndi mpongozi wakeyo.
So she kept close company with the maidens of Bo'az in gleaning until the end of the barley-harvest and of the wheat-harvest; and she dwelt with her mother-in-law.

< Rute 2 >