< Rute 2 >

1 Naomi anali ndi mʼbale wake wolemera kwambiri wochokera ku banja la mwamuna wake Elimeleki, dzina lake Bowazi.
But there was a man related to Elimelech, a powerful man, and very wealthy, named Boaz.
2 Tsiku lina Rute, Mmowabu uja anati kwa Naomi, “Mundilole kuti ndikakunkhe barele ku munda wa munthu aliyense amene akandikomere mtima.” Naomi anati kwa iye, “Pita mwana wanga.”
And Ruth, the Moabite, said to her mother-in-law, “If you order, I will go into the field and gather the ears of grain which escape the reaping hand, wherever I will find favor with the father of a family, who will be compassionate to me.” She answered her, “Go, my daughter.”
3 Choncho Rute ananyamuka kupita kukakunkha ku minda yokololedwa kale. Tsono zinangochitika kuti Rute anafika mʼmunda wa Bowazi, yemwe anali wochokera ku banja la Elimeleki.
And so she went and gathered the ears of grain after the completion of the reaping. But it happened that this field was owned by Boaz, who was of the kindred of Elimelech.
4 Posakhalitsa Bowazi anafika kuchokera ku Betelehemu ndipo analonjera okolola aja kuti, “Yehova akhale nanu!” Iwo anayankha kuti, “Yehova akudalitseni.”
And behold, he came out of Bethlehem and said to the reapers, “The Lord be with you.” They answered him, “May the Lord bless you.”
5 Bowazi anafunsa kapitawo wake amene ankayangʼanira okolola aja kuti, “Mayi uyo ndi ndani?”
And Boaz said to the young man who was in charge of the reapers, “Whose young woman is this?”
6 Kapitawo uja anayankha kuti, “Mayiyu ndi Mmowabu amene anabwera ndi Naomi kuchokera ku dziko la Mowabu.
He answered him, “This is the Moabite woman, who came with Naomi, from the land of the Moabites,
7 Iye anandipempha kuti, ‘Chonde mundilole kuti ndikunkhe barele mʼminda moti akololamo kale.’ Iye wakhala akukunkha kuyambira mmawa mpaka tsopano lino osapuma nʼpangʼono pomwe.”
and she asked to gather the remnants of the ears of grain, following the steps of the reapers, and from morning until now she has remained in the field, and, indeed, not for one moment has she returned home.”
8 Choncho Bowazi anati kwa Rute, “Tamvera mwana wanga, usapite kukakunkha mʼmunda wina, ndipo usachoke mʼmunda uno. Koma uzitsata adzakazi angawa.
And Boaz said to Ruth, “Listen to me, daughter. Do not go to gather in any other field, nor depart from this place, but join with my young women,
9 Uziyangʼana munda akukolola anyamatawo akamakolola mʼmundamu, ndipo iwe uzitsata pambuyo pawo. Ndawawuza anyamatawo kuti asakuvutitse. Ndipo ukamva ludzu, uzipita ku mitsuko ndi kukamwa madzi amene anyamatawa atunga.”
and follow where they reap. For I have given orders to my young men, so that no one is to harass you. And so, whenever you are thirsty, go to the vessels, and drink from the waters that the young men also drink.”
10 Atamva zimenezi Rute anawerama nazolikitsa nkhope yake pansi. Kenaka anafunsa kuti, “Mwandikomera mtima chotere mlendo ngati ine chifukwa chiyani?”
She, falling on her face and paying homage on the ground, said to him: “How did this happen to me, that I should find favor before your eyes, and that you would condescend to accept me, a foreign woman?”
11 Bowazi anayankha kuti, “Ine ndawuzidwa zonse zimene wakhala ukuchitira apongozi ako chimwalirire mwamuna wako. Ndamvanso kuti unasiya abambo ndi amayi ako komanso dziko la kwanu ndi kubwera kudzakhala ndi anthu amene sumawadziwa ndi kale lonse.
He answered her, “Everything has been reported to me, what things you have done for your mother-in-law after the death of your husband, and how you left your parents, and the land in which you were born, and came to a people you did not know before.
12 Yehova akubwezere pa zimene wachitazi. Yehova Mulungu wa Israeli, amene wabwera pansi pa mapiko ake kuti akuteteze, akupatse mphotho yayikulu.”
May the Lord repay you for your work, and may you receive a full reward from the Lord, the God of Israel, to whom you have come, and under whose wings you have taken refuge.”
13 Rute anati, “Mwandikomera mtima, mbuye wanga. Ndipo mwandisangalatsa ndi kundiyankhula mwa chifundo ngakhale sindili mmodzi mwa adzakazi anu.”
She said, “I have found favor before your eyes, my lord, who has consoled me, and you have spoken to the heart of your handmaid, who is unlike one of your young women.”
14 Nthawi ya chakudya cha masana Bowazi anati kwa iye, “Bwera kuno, utenge buledi ndi kusunsa nthongo mu vinyo.” Choncho anakhala pansi pafupi ndi okololawo, ndipo Bowazi anamupatsa chakudya ndi nyama yowotcha. Anadya chilichonse amafuna ndipo chakudya china chinatsalako.
And Boaz said to her, “When mealtime begins, come here, and eat bread, and dip your morsel in the vinegar.” And so she sat beside the reapers, and she piled up parched grain for herself, and she ate and was satisfied, and carried off the leftovers.
15 Atanyamuka kuti azikakunkha, Bowazi analangiza anyamata ake kuti, “Ngakhale mayiyu azikunkha pakati pa mitolo musamuletse ndi kumuchititsa manyazi.
And then she arose from there, so as to gather the ears of grain, according to the custom. But Boaz commanded his servants, saying, “If she is even willing to reap with you, do not prevent her,
16 Koma muzimusololerako ngala zina za mʼmitolo ndi kumusiyira kuti azikunkha ndipo musamukalipire.”
and purposely let fall some from your bundles, and allow them to remain, so that she may gather without blushing, and let no one rebuke her gathering.”
17 Choncho Rute anakunkha mʼmundamo mpaka madzulo. Kenaka anapuntha barele anakunkhayo, ndipo anakwanira pafupifupi makilogalamu khumi.
And so she gathered in the field until evening. And striking and threshing with a staff what she had gathered, she found about the measure of an ephah of barley, that is, three measures.
18 Anasenza barele uja kupita naye ku mudzi, nakaonetsa apongozi ake. Kenaka anatulutsa chakudya chimene chinatsalira atakhuta chija ndi kupatsa apongozi ake.
Carrying this, she returned into the city and showed it to her mother-in-law. Moreover, she offered it to her and even gave her the leftovers of her food, with which she had been satisfied.
19 Apongozi akewo anamufunsa kuti, “Kodi lero unakakunkha kuti? Unakagwira kuti ntchitoyi? Adalitsike munthu amene anakukomera mtimayo.” Ndipo Rute anawuza mpongozi wake za munthu amene ku malo ake anakagwirako ntchito. Iye anati, “Munthuyo dzina lake ndi Bowazi.”
And her mother-in-law said to her, “Where have you gathered today, and where have you found work? Blessed is he who took pity on you!” And she informed her with whom she had been working, and she said the man’s name, that he was called Boaz.
20 Naomi anati kwa mpongozi wakeyo, “Munthu ameneyu amudalitse Yehova, amene sanasiye kuchitira chifundo anthu amoyo ndi akufa omwe. Anatinso munthu ameneyu ndi mnansi wapaphata. Ndiye ali ndi udindo wotisamalira.”
Naomi answered her, “May he be blessed by the Lord, because the same kindness which he provided for the living, he also kept for the dead.” And again she said: “This man is our near relative.”
21 Choncho Rute Mmowabuyo anati, “Iye anandiwuzanso kuti, ‘Uzitsata antchito angawa mpaka atamaliza kukolola munda wonse.’”
And Ruth said, “He charged me with this also, that from now on I should join with his reapers until all the crop has been reaped.”
22 Naomi anati kwa Rute mpongozi wake, “Kuli bwino mwana wanga kuti uzipita ndi adzakazi ake kuopa kuti mʼmunda wa munthu wina angakuvute.”
And her mother-in-law said to her, “It is better, my daughter, to go out reaping with his young women, lest in a stranger’s field someone may confront you.”
23 Choncho Rute ankatsatira adzakazi a Bowazi namakunkha mpaka anthu atamaliza kudula barele ndi tirigu. Ndipo amakhalabe ndi mpongozi wakeyo.
And so, she joined with the young women of Boaz, and from then on reaped with them, until the barley and the wheat were stored in the barns.

< Rute 2 >