< Rute 2 >
1 Naomi anali ndi mʼbale wake wolemera kwambiri wochokera ku banja la mwamuna wake Elimeleki, dzina lake Bowazi.
Měla pak Noémi přítele po manželu svém, muže mocného z čeledi Elimelechovy, jménem Bóza.
2 Tsiku lina Rute, Mmowabu uja anati kwa Naomi, “Mundilole kuti ndikakunkhe barele ku munda wa munthu aliyense amene akandikomere mtima.” Naomi anati kwa iye, “Pita mwana wanga.”
I řekla Rut Moábská Noémi: Nechť medle jdu na pole sbírati klasů za tím, kdož by mi toho přál. Jížto ona řekla: Jdi, dcero má.
3 Choncho Rute ananyamuka kupita kukakunkha ku minda yokololedwa kale. Tsono zinangochitika kuti Rute anafika mʼmunda wa Bowazi, yemwe anali wochokera ku banja la Elimeleki.
Šla tedy, a přišedši, sbírala klasy na poli za ženci. Přihodilo se pak, že přišla na díl pole toho, kteréž přináleželo Bózovi, jenž byl z čeledi Elimelechovy.
4 Posakhalitsa Bowazi anafika kuchokera ku Betelehemu ndipo analonjera okolola aja kuti, “Yehova akhale nanu!” Iwo anayankha kuti, “Yehova akudalitseni.”
A v tom přišel Bóz z Betléma, a řekl žencům: Hospodin s vámi. Kteříž odpověděli jemu: Požehnejž tobě Hospodin.
5 Bowazi anafunsa kapitawo wake amene ankayangʼanira okolola aja kuti, “Mayi uyo ndi ndani?”
I řekl Bóz služebníku svému, kterýž postaven byl nad ženci: Èí jest tato mladice?
6 Kapitawo uja anayankha kuti, “Mayiyu ndi Mmowabu amene anabwera ndi Naomi kuchokera ku dziko la Mowabu.
Odpověděl služebník ten, kterýž postaven byl nad ženci, a řekl: Jest mladice Moábská, kteráž přišla s Noémi z země Moábské.
7 Iye anandipempha kuti, ‘Chonde mundilole kuti ndikunkhe barele mʼminda moti akololamo kale.’ Iye wakhala akukunkha kuyambira mmawa mpaka tsopano lino osapuma nʼpangʼono pomwe.”
A řekla mi: Prosím, nechť sbírám a shromažďuji klasy mezi snopy za ženci. A přišedši, trvá od jitra až dosavad, kromě že na chvilku doma pobyla.
8 Choncho Bowazi anati kwa Rute, “Tamvera mwana wanga, usapite kukakunkha mʼmunda wina, ndipo usachoke mʼmunda uno. Koma uzitsata adzakazi angawa.
Tedy řekl Bóz k Rut: Slyš, dcero má, nechoď sbírati na jiné pole, aniž odcházej odsud, ale přídrž se teď děvek mých.
9 Uziyangʼana munda akukolola anyamatawo akamakolola mʼmundamu, ndipo iwe uzitsata pambuyo pawo. Ndawawuza anyamatawo kuti asakuvutitse. Ndipo ukamva ludzu, uzipita ku mitsuko ndi kukamwa madzi amene anyamatawa atunga.”
Zůstávej na tom poli, na němž budou žíti, a choď za nimi, nebo jsem přikázal služebníkům svým, aby se tebe žádný nedotýkal. Bude-liť se chtíti píti, jdi k nádobám, a napí se té vody, kteréž by navážili služebníci moji.
10 Atamva zimenezi Rute anawerama nazolikitsa nkhope yake pansi. Kenaka anafunsa kuti, “Mwandikomera mtima chotere mlendo ngati ine chifukwa chiyani?”
Tedy ona padla na tvář svou, a schýlivši se k zemi, řekla jemu: Odkudž mi to, že jsem nalezla milost před tebou, abys se známil ke mně, kteráž jsem cizozemka.
11 Bowazi anayankha kuti, “Ine ndawuzidwa zonse zimene wakhala ukuchitira apongozi ako chimwalirire mwamuna wako. Ndamvanso kuti unasiya abambo ndi amayi ako komanso dziko la kwanu ndi kubwera kudzakhala ndi anthu amene sumawadziwa ndi kale lonse.
Odpověděl Bóz a řekl: O všemť mi oznámeno jest, co jsi koli činila svegruši své po smrti muže svého, a že opustivši otce svého a matku svou, i zemi, v kteréžs se narodila, šla jsi mezi lid, kteréhožs prvé neznala.
12 Yehova akubwezere pa zimene wachitazi. Yehova Mulungu wa Israeli, amene wabwera pansi pa mapiko ake kuti akuteteze, akupatse mphotho yayikulu.”
Odplatiž tobě Hospodin za skutek tvůj, a budiž mzda tvá dokonalá od Hospodina Boha Izraelského, poněvadž jsi přišla, abys pod křídly jeho doufala.
13 Rute anati, “Mwandikomera mtima, mbuye wanga. Ndipo mwandisangalatsa ndi kundiyankhula mwa chifundo ngakhale sindili mmodzi mwa adzakazi anu.”
Kterážto řekla: Nalezla jsem milost před tebou, pane můj, poněvadž jsi mne potěšil, a mluvils k srdci děvky své, ješto nejsem podobná jedné z děvek tvých.
14 Nthawi ya chakudya cha masana Bowazi anati kwa iye, “Bwera kuno, utenge buledi ndi kusunsa nthongo mu vinyo.” Choncho anakhala pansi pafupi ndi okololawo, ndipo Bowazi anamupatsa chakudya ndi nyama yowotcha. Anadya chilichonse amafuna ndipo chakudya china chinatsalako.
Tedy řekl jí Bóz: Když bude čas jísti, přistup sem, a pojez chleba, a omoč skyvu svou v octě. I posadila se při žencích, a podal jí pražmy; ona pak jedla až do sytosti, a ještě jí zbylo.
15 Atanyamuka kuti azikakunkha, Bowazi analangiza anyamata ake kuti, “Ngakhale mayiyu azikunkha pakati pa mitolo musamuletse ndi kumuchititsa manyazi.
I vstala, aby sbírala. Přikázal pak Bóz služebníkům svým, řka: Byť pak i mezi snopy sbírala, nezbraňujte jí.
16 Koma muzimusololerako ngala zina za mʼmitolo ndi kumusiyira kuti azikunkha ndipo musamukalipire.”
Nýbrž naschvál jí upouštějte z snopů a nechávejte, ať sbírá, a nedomlouvejte jí.
17 Choncho Rute anakunkha mʼmundamo mpaka madzulo. Kenaka anapuntha barele anakunkhayo, ndipo anakwanira pafupifupi makilogalamu khumi.
Sbírala tedy na poli tom až do večera, a což sebrala, to vymlátila; i byla téměř míra efi ječmene.
18 Anasenza barele uja kupita naye ku mudzi, nakaonetsa apongozi ake. Kenaka anatulutsa chakudya chimene chinatsalira atakhuta chija ndi kupatsa apongozi ake.
Kterýž vzavši, přišla do města, a viděla svegruše její to, což nasbírala. Vyňala také a dala jí to, což pozůstalo po nasycení jejím.
19 Apongozi akewo anamufunsa kuti, “Kodi lero unakakunkha kuti? Unakagwira kuti ntchitoyi? Adalitsike munthu amene anakukomera mtimayo.” Ndipo Rute anawuza mpongozi wake za munthu amene ku malo ake anakagwirako ntchito. Iye anati, “Munthuyo dzina lake ndi Bowazi.”
I řekla jí svegruše její: Kdes sbírala dnes, a kdes pracovala? Budiž požehnaný ten, kterýž tě přijal. Tedy oznámila svegruši své, u koho pracovala, řkuci: Jméno muže, u kteréhož jsem pracovala dnes, jest Bóz.
20 Naomi anati kwa mpongozi wakeyo, “Munthu ameneyu amudalitse Yehova, amene sanasiye kuchitira chifundo anthu amoyo ndi akufa omwe. Anatinso munthu ameneyu ndi mnansi wapaphata. Ndiye ali ndi udindo wotisamalira.”
I řekla Noémi nevěstě své: Požehnanýť jest od Hospodina, že nepřestal milosrdenství svého nad živými i mrtvými. I to ještě k ní řekla Noémi: Blízký přítel náš a z příbuzných našich jest muž ten.
21 Choncho Rute Mmowabuyo anati, “Iye anandiwuzanso kuti, ‘Uzitsata antchito angawa mpaka atamaliza kukolola munda wonse.’”
Řekla jí také Rut Moábská: I to mi ještě řekl: Èeládky mé přídrž se, dokavadž by všeho, což mého jest, nedožali.
22 Naomi anati kwa Rute mpongozi wake, “Kuli bwino mwana wanga kuti uzipita ndi adzakazi ake kuopa kuti mʼmunda wa munthu wina angakuvute.”
Tedy řekla Noémi Rut nevěstě své: Dobré jest tedy, dcero má, abys vycházela s děvečkami jeho, ať by na jiném poli něco nepřekazili.
23 Choncho Rute ankatsatira adzakazi a Bowazi namakunkha mpaka anthu atamaliza kudula barele ndi tirigu. Ndipo amakhalabe ndi mpongozi wakeyo.
A tak se přídržela Rut děvek Bózových, a sbírala klasy, dokudž nesžali ječmene a pšenice, a bydlela u svegruše své.